Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 5/07 tsamba 4
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2007
  • Nkhani Yofanana
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2009
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2009
  • Zimene Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2010
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2011
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2007
km 5/07 tsamba 4

Zomwe Munganene Pogawira Magazini

Nsanja ya Olonda May 15

“Kodi mungayankhe bwanji funso ili? [Werengani funso la pachikuto. Ndiyeno yembekezerani ayankhe.] Mfundo za m’Baibulo zimatipatsa chiyembekezo. [Werengani Mateyo 6:9, 10.] Magazini iyi ikufotokoza zimene Ufumu wa Mulungu udzachite pokwaniritsa chifuniro cha Mulungu padziko lapansi.”

Galamukani! May

“Kodi mukuganiza kuti Mulungu analemberatu zochita zathu ndiponso tsogolo lathu lonse? [Yembekezerani ayankhe.] Vesi ili likusonyeza kuti Mulungu amalola anthu kusankha okha tsogolo lawo. [Werengani Deuteronomo 30:19.] Mutu uwu ukufotokoza zimene Baibulo limanena pa nkhaniyi.” Asonyezeni nkhani imene yayambira pa tsamba 12.

Nsanja ya Olonda June 1

“Pafupifupi tsiku lililonse timamva nkhani za anthu amene amachita zoipa. [Tchulani zimene zangochitika kumene komanso zimene zikudziwika m’dera lanulo.] Kodi munayamba mwaganizapo kuti pali mzimu winawake woipa umene umachititsa anthu zoipazi? [Yembekezani ayankhe. Ndiyeno werengani Chivumbulutso 12:12.] Magaziniyi ikulongosola mmene tingadzitetezere.”

Galamukani! June

“Ndikufuna ndimve maganizo anu pa zimene lemba ili likunena. [Werengani 1 Timoteyo 6:10.] Kodi mukuvomereza kuti anthu amene amakonda kwambiri ndalama ndi chuma amagwadi m’mavuto chifukwa cha zimenezi? [Yembekezani ayankhe.] Magaziniyi ikufotokoza mavuto amene munthu angagwemo chifukwa chofunafuna kwambiri chuma.”

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena