Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 5/06 tsamba 4
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2006
  • Nkhani Yofanana
  • Zitsanzo za Ulaliki
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2011
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2004
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2007
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2009
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2006
km 5/06 tsamba 4

Zomwe Munganene Pogawira Magazini

Nsanja ya Olonda May 15

“Kodi mukuganiza kuti mungasangalale kukhala ndi moyo zinthu zitakhala kuti zili monga mmene zafotokozedwera pa lemba louziridwa ili? [Werengani 2 Pet. 3:13. Ndiyeno yembekezani ayankhe.] Magazini iyi ikufotokoza tanthauzo la miyamba yatsopano ndi dziko latsopano. Ikufotokozanso mmene moyo udzasinthira Mulungu akadzakwaniritsa zolinga zake zokhudza dziko lapansi.”

Galamukani! May

“Anthu ena amakhulupirira kuti ngati munthu ali wofatsa zinthu sizingamuyendere masiku ano. Mosiyana ndi maganizo amenewa, onani zimene Yesu ananena. [Werengani Mateyu 5:5, 9.] Kodi mukuvomereza zimenezi? [Yembekezani ayankhe.] Magazini iyi ikusonyeza kuti tingapindule m’njira zitatu, ngati titakhala anthu amtendere.” Sonyezani nkhani yomwe yayambira patsamba 28.

Nsanja ya Olonda June 1

“Nthawi inayake anthu amitundu yambiri ankalemekeza anthu okalamba, monga mmene tingaonere ndi lamulo lakalekale ili. [Werengani Levitiko 19:32.] Kodi ulemu wotere ndi wofala masiku ano? [Yembekezani ayankhe.] Magaziniyi ikufotokoza mmene Mulungu amasamalira anthu okalamba ndi mmene ifenso tingachitire zimenezo.”

Galamukani! June

“Uchigawenga sunayambe lero, koma masiku ano wakula kwambiri ndipo ukukhudza aliyense padziko lonse lapansi. Kodi n’chifukwa chiyani zili choncho? [Yembekezani ayankhe.] Galamukani! ino ikutchula nthawi imene uchigawenga udzatha ndiponso mmene Mulungu adzabweretsera mtendere weniweni padziko lapansi.” Werengani Mika 4:4.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena