Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb16 October tsamba 4
  • Zimene Tingachite Kuti Ndemanga Zathu Zizikhala Zabwino

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zimene Tingachite Kuti Ndemanga Zathu Zizikhala Zabwino
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2016
  • Nkhani Yofanana
  • Tizitamanda Yehova Mumpingo
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2019
  • Tizilimbikitsana Pamisonkhano ya Mpingo
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2023
  • Tamandani Yehova “Pakati pa Msonkhano”
    Nsanja ya Olonda—2003
  • Gwiritsani Chilengezo Chapoyera cha hiyembekezo Chanu Mosagwedera
    Utumiki Wathu wa Ufumu—1994
Onani Zambiri
Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2016
mwb16 October tsamba 4

MOYO WATHU WACHIKHRISTU

Zimene Tingachite Kuti Ndemanga Zathu Zizikhala Zabwino

Mnyamata wakweza dzanja paphunziro la Nsanja ya Olonda, mlongo akuyankha paphunziro la Nsanja ya Olonda

Ndemanga zabwino zimalimbikitsa mpingo komanso zimathandiza anthu omwe amazipereka. (Miy. 15:23, 28; Aroma 14:19) N’chifukwa chake tiyenera kumayesetsa kupereka ndemanga pamsonkhano uliwonse. Komabe sikuti tingapatsidwe mwayi woyankha nthawi iliyonse imene takweza mkono. Choncho tingachite bwino kumakonzekera ndemanga zingapo.

Ndemanga yabwino imakhala . . .

  • yosavuta, yomveka bwino komanso yachidule. Nthawi zambiri ikhoza kukhala yosapitirira masekondi 30

  • imene mwaifotokoza m’mawu anuanu

  • imene sikungobwereza zimene anthu ena ayankha kale

Ngati ndinu woyamba kuyankha funso linalake, . . .

  • mungoyankha funsolo mwachidule popanda kufotokoza zambiri

Ngati funso layankhidwa kale, mukhoza . . .

  • kusonyeza mmene lemba lina la mundimeyo likugwirizanira ndi mfundo za mundimeyo

  • kufotokoza mmene mfundozo zingatithandizire

  • kufotokoza mmene tingagwiritsire ntchito mfundozo

  • kufotokoza mwachidule chitsanzo chogwirizana ndi mfundo yaikulu ya mundimeyo

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena