Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb17 June tsamba 3
  • Nthawi Zonse Mawu a Yehova Amakwaniritsidwa

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Nthawi Zonse Mawu a Yehova Amakwaniritsidwa
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2017
  • Nkhani Yofanana
  • Babulo Wamphamvu—Mphamvu Yaikulu ya Dziko Yachitatu
    Nsanja ya Olonda—1988
  • Baibulo ndi Buku la Maulosi Olondola Gawo 2
    Galamukani!—2012
  • Buku la Ulosi
    Buku la Anthu Onse
Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2017
mwb17 June tsamba 3

CHUMA CHOPEZEKA M’MAWU A MULUNGU | YEREMIYA 51–52

Nthawi Zonse Mawu a Yehova Amakwaniritsidwa

Yehova ananeneratu molondola zinthu zam’tsogolo

Msilikali wachiperisiya

Msilikali wachiperisiya

“Nolani mivi yanu”

51:11, 28

  • Amedi ndi Aperisi anali akatswiri oponya mivi ndipo ankadalira kwambiri mauta. Iwo ankanola mivi yawo kuti akabaya izilowa mkati kwambiri

“Amuna amphamvu a ku Babulo asiya kumenya nkhondo”

51:30

  • Mbiri ya Nabonidus imati: “Magulu a nkhondo a Koresi analowa m’Babulo popanda kumenya nkhondo.” Izi zikutanthauza kuti Koresi analowa mumzinda wa Babulo popanda wolimbana naye ndipo n’zogwirizana ndi zimene ulosi wa Yeremiya unanena

Mbiri ya Nabonidus

Mbiri ya Nabonidus

“Babulo adzakhala milu yamiyala [ndiponso] bwinja mpaka kalekale”

51:37, 62

  • Kuyambira m’chaka cha 539 B.C.E., ulemerero wa Babulo unayamba kuchepa. Alekizanda Wamkulu ankafuna kuti mzinda wa Babulo ukhale likulu la ulamuliro wake, koma pasanapite nthawi anamwalira. Chikhristu chitangoyamba kumene, mtumwi Petulo ankafika ku Babulo chifukwa kunali Ayuda ena omwe ankakhala kumeneko. Koma pofika m’zaka za m’ma 300 C.E., mzindawo unawonongedwa ndipo sunakhaleponso

    Tchati chosonyeza nthawi imene Babulo anagonjetsedwa, kufa kwa Alekizanda Wamkulu, Petulo ali ku Babulo ndi mabwinja a Babulo

Kodi kukwaniritsidwa kwa maulosi a m’Baibulo kungandithandize bwanji?

Kodi ndingaphunzitse ena chiyani zokhudza ulosiwu?

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena