Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb18 June tsamba 7
  • Muzisamala Mukamacheza ndi Anzanu pa Intaneti

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Muzisamala Mukamacheza ndi Anzanu pa Intaneti
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2018
  • Nkhani Yofanana
  • Kodi Mumacheza ndi Ndani pa Intaneti?
    Kabuku ka Msonkhano wa Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—2022
  • N’chifukwa Chiyani Anthu Ambiri Amakonda Kuwagwiritsa Ntchito?
    Galamukani!—2012
  • Mfundo Zinayi Zimene Muyenera Kudziwa Zokhudza Malo Amenewa
    Galamukani!—2012
  • Kodi Malo Ochezera a pa Intaneti Akusokoneza Moyo Wanga?
    Zimene Achinyamata Amafunsa
Onani Zambiri
Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2018
mwb18 June tsamba 7

MOYO WATHU WACHIKHRISTU

Muzisamala Mukamacheza ndi Anzanu pa Intaneti

Yesu akukana kusandutsa miyala kukhala mikate

N’CHIFUKWA CHIYANI M’POFUNIKA KUSAMALA? Monga mmene zilili ndi zipangizo zambiri zomwe zingakuthandizeni kapena kukuvulazani, malo ochezera a pa intaneti angakhale abwino kapena oipa malinga ndi mmene tikuwagwiritsira ntchito. Akhristu ena amasankha kusagwiritsa ntchito malo amenewa. Pomwe ena amagwiritsa ntchito malowa pocheza komanso kulankhulana ndi achibale ndiponso anzawo. Koma Satana amafuna kuti tizigwiritsa ntchito malowa molakwika ndipo zimenezi zingaipitse mbiri ya munthu komanso zingawononge ubwenzi wake ndi Yehova. Mofanana ndi Yesu, nafenso tikhoza kugwiritsa ntchito mfundo za m’Mawu a Mulungu kuti tizindikire mayesero komanso kuwapewa.​—Luka 4:4, 8, 12.

ZINTHU ZIMENE MUYENERA KUSAMALA NAZO:

  • Kutha nthawi yaitali mukucheza pa intaneti. Tikamathera nthawi yambiri tikucheza ndi anthu pa intaneti, tingamalephere kuchita zinthu zomwe zingalimbitse ubwenzi wathu ndi Yehova

    Mfundo za m’Baibulo: Aef. 5:15, 16; Afil. 1:10

  • Kuona kapena kuwerenga zinthu zoipa. Kuona zithunzi zosonyeza anthu atavala mosayenera kungachititse kuti munthu ayambe kuonera zolaula kapena kuchita chiwerewere. Kuwerenga mabuku kapena nkhani zimene anthu ampatuko amalemba pa intaneti kungawononge chikhulupiriro chathu

    Mfundo za m’Baibulo: Mat. 5:28; Afil. 4:8

  • Kuika zithunzi zosayenera komanso kulemba makomenti oipa. Popeza mtima ndi wonyenga, munthu akhoza kuika zithunzi zosayenera kapena kulemba makomenti oipa pamalo ochezera a pa intaneti. Koma zimenezi zikhoza kuwononga mbiri ya munthu komanso zingachititse kuti asokoneze ubwenzi wake ndi Yehova

    Mfundo za m’Baibulo: Aroma 14:13; Aef. 4:29

ONERANI VIDIYO YAKUTI MUZICHITA ZINTHU MWANZERU MUKAMACHEZA NDI ANZANU PA INTANETI, KENAKO ONANI MMENE MUNGAPEWERE MAVUTO OMWE AKUSONYEZEDWA M’ZITHUNZIZI:

Mbala yadziwa kudzera pamalo ochezera kuti eni ake nyumba apita ku tchuthi
Bwana akutha kuona zithunzi zosayenera za munthu amene akufuna kumulemba ntchito
Akuona ma komenti oipa a anthu ena
Munthu akukanika kudzuka chifukwa chocheza pa intaneti usiku wonse
    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena