Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb19 June tsamba 8
  • Muzipindula Mokwanira Mukamaphunzira Panokha

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Muzipindula Mokwanira Mukamaphunzira Panokha
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2019
  • Nkhani Yofanana
  • Kuphunzira Kumapindulitsa
    Pindulani ndi Sukulu ya Utumiki wa Mulungu
  • Kuphunzira—N’kothandiza ndi Kokondweretsa
    Nsanja ya Olonda—2000
  • Tsanzirani Chitsanzo cha Mfumu
    Nsanja ya Olonda—2002
  • Kupanga Ubwenzi Wolimba ndi Yehova
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2003
Onani Zambiri
Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2019
mwb19 June tsamba 8

MOYO WATHU WACHIKHRISTU

Muzipindula Mokwanira Mukamaphunzira Panokha

KODI ZIMENEZI N’ZOFUNIKA BWANJI? Tikamaphunzira Mawu a Mulungu patokha, timadziwa bwino “m’lifupi ndi m’litali ndi kukwera ndi kuzama” kwa choonadi. (Aef. 3:18) Kuphunzira patokha kumatithandiza kuti tikhale osalakwa komanso opanda chilema m’dziko loipali. Kumatithandizanso kuti tipitirize “kugwira mwamphamvu mawu amoyo.” (Afil. 2:15, 16) Tikamaphunzira Mawu a Mulungu timatha kusankha zomwe tikufuna kuphunzira malinga ndi zimene tikufunikira. Kodi tingatani kuti tizipindula kwambiri tikamawerenga komanso kuphunzira Baibulo?

KODI TINGACHITE BWANJI ZIMENEZI?

  • Muzilemba mzere kunsi kwa mavesi komanso notsi m’Baibulo lanu

  • Mukamawerenga Mawu a Mulungu muzidzifunsa mafunso monga akuti: ‘Nkhaniyi ikunena za ndani? Chinachitika n’chiyani? Zinachitikira kuti? Zinachitika bwanji? N’chifukwa chiyani zinachitika choncho?’

  • Muzifufuza. Mungagwiritse ntchito zipangizo zofufuzira zimene muli nazo ndipo mukhoza kufufuza pogwiritsa ntchito mitu ya nkhani kapena mavesi a m’Baibulo

  • Muziganizira mozama zimene mwawerengazo n’kuona mmene zikukukhudzirani

  • Muzigwiritsa ntchito zimene mwaphunzira.​—Luka 6:47, 48

ONERANI VIDIYO YAKUTI PITIRIZANI “KUGWIRA MWAMPHAMVU MAWU AMOYO” POPHUNZIRA MWAKHAMA, KENAKO YANKHANI MAFUNSO OTSATIRAWA:

  • Kodi ena apindula bwanji chifukwa chophunzira pawokha?

  • N’chifukwa chiyani tiyenera kupemphera tisanayambe kuphunzira patokha?

  • Kodi n’chiyani chingatithandize kuti tizimvetsa bwino zimene tikuwerenga m’Baibulo?

  • Kodi ndi zizindikiro ziti zomwe tingalembe m’Baibulo lathu tikamaphunzira patokha?

  • Kodi kuganizira zomwe tikuwerenga n’kofunika bwanji?

  • N’chifukwa chiyani tiyenera kugwiritsa ntchito zimene taphunzira?

Mlongo akuphunzira Baibulo payekha; m’bale wachekenira mavesi ena m’Baibulo lake; mlongo akuonetsa abale awiri notsi zomwe analemba m’Baibulo lake; m’bale akupemphera

“Ndimakonda kwambiri chilamulo chanu! Ndimasinkhasinkha chilamulocho tsiku lonse.”​—Sal. 119:97

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena