MOYO WATHU WACHIKHRISTU
Muzipindula Mokwanira Mukamaphunzira Panokha
KODI ZIMENEZI N’ZOFUNIKA BWANJI? Tikamaphunzira Mawu a Mulungu patokha, timadziwa bwino “m’lifupi ndi m’litali ndi kukwera ndi kuzama” kwa choonadi. (Aef. 3:18) Kuphunzira patokha kumatithandiza kuti tikhale osalakwa komanso opanda chilema m’dziko loipali. Kumatithandizanso kuti tipitirize “kugwira mwamphamvu mawu amoyo.” (Afil. 2:15, 16) Tikamaphunzira Mawu a Mulungu timatha kusankha zomwe tikufuna kuphunzira malinga ndi zimene tikufunikira. Kodi tingatani kuti tizipindula kwambiri tikamawerenga komanso kuphunzira Baibulo?
KODI TINGACHITE BWANJI ZIMENEZI?
Muzilemba mzere kunsi kwa mavesi komanso notsi m’Baibulo lanu
Mukamawerenga Mawu a Mulungu muzidzifunsa mafunso monga akuti: ‘Nkhaniyi ikunena za ndani? Chinachitika n’chiyani? Zinachitikira kuti? Zinachitika bwanji? N’chifukwa chiyani zinachitika choncho?’
Muzifufuza. Mungagwiritse ntchito zipangizo zofufuzira zimene muli nazo ndipo mukhoza kufufuza pogwiritsa ntchito mitu ya nkhani kapena mavesi a m’Baibulo
Muziganizira mozama zimene mwawerengazo n’kuona mmene zikukukhudzirani
Muzigwiritsa ntchito zimene mwaphunzira.—Luka 6:47, 48
ONERANI VIDIYO YAKUTI PITIRIZANI “KUGWIRA MWAMPHAMVU MAWU AMOYO” POPHUNZIRA MWAKHAMA, KENAKO YANKHANI MAFUNSO OTSATIRAWA:
Kodi ena apindula bwanji chifukwa chophunzira pawokha?
N’chifukwa chiyani tiyenera kupemphera tisanayambe kuphunzira patokha?
Kodi n’chiyani chingatithandize kuti tizimvetsa bwino zimene tikuwerenga m’Baibulo?
Kodi ndi zizindikiro ziti zomwe tingalembe m’Baibulo lathu tikamaphunzira patokha?
Kodi kuganizira zomwe tikuwerenga n’kofunika bwanji?
N’chifukwa chiyani tiyenera kugwiritsa ntchito zimene taphunzira?
“Ndimakonda kwambiri chilamulo chanu! Ndimasinkhasinkha chilamulocho tsiku lonse.”—Sal. 119:97