MOYO WATHU WACHIKHRISTU
Kodi Maganizo a Yehova Ndi Otani pa Nkhaniyi?
Tisanasankhe zochita pa nkhani iliyonse, kaya yaikulu kapena yaing’ono, tizidzifunsa kuti, ‘Kodi maganizo a Yehova ndi otani pa nkhaniyi?’ Ngakhale kuti sitingadziwe zonse zokhudza mmene Yehova amaganizira, Mawu ake angatithandize kuti tichite “ntchito iliyonse yabwino.” (2 Tim. 3:16, 17; Aroma 11:33, 34) Yesu ankadziwa bwino zimene Yehova amafuna ndipo ankachita zimenezo pa moyo wake. (Yoh. 4:34) Ifenso tiziyesetsa kutsanzira Yesu posankha zinthu zimene zingasangalatse Yehova.—Yoh. 8:28, 29; Aef. 5:15-17.
ONERANI VIDIYO YAKUTI PITIRIZANI KUZINDIKIRA CHIFUNIRO CHA YEHOVA (LEV. 19:18), KENAKO YANKHANI MAFUNSO OTSATIRAWA:
N’chifukwa chiyani tiyenera kugwiritsa ntchito mfundo za m’Baibulo pa moyo wathu?
Kodi muyenera kuganizira mfundo za m’Baibulo ziti mukamasankha nyimbo?
Kodi muyenera kuganizira mfundo za m’Baibulo ziti pa nkhani ya zovala komanso kudzikongoletsa?
Kodi ndi pa nkhani zinanso ziti pomwe tingafunike kugwiritsa ntchito mfundo za m’Baibulo?
Kodi tingatani kuti tizidziwa bwino zimene Yehova amafuna kuti tizichita?
Zimene timasankha zimasonyeza mmene ubwenzi wathu ndi Yehova ulili