Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb19 October tsamba 8
  • Yehova Amakonda Anthu Aukhondo

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Yehova Amakonda Anthu Aukhondo
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2019
  • Nkhani Yofanana
  • Kodi Ukhondo Umatanthauza Chiyani Makamaka?
    Nsanja ya Olonda—2002
  • Kodi Ukhondo Ndi Wofunika Motani?
    Nsanja ya Olonda—2002
  • Mulungu Amakonda Anthu Oyera
    Kodi Mungatani Kuti ‘Mulungu Apitirize Kukukondani’?
  • N’chifukwa Chiyani Ukhondo Uli Wofunika?
    Nsanja ya Olonda—2008
Onani Zambiri
Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2019
mwb19 October tsamba 8
M’bale akukonza kuzimbudzi pa Nyumba ya Ufumu

MOYO WATHU WACHIKHRISTU

Yehova Amakonda Anthu Aukhondo

Makolo ambiri amakonda kuuza ana awo kuti, ‘Kasambeni m’manja. Kakonzeni kuchipinda kwanu. Kaseseni panja. Katayeni zinyalala.’ Amanena zimenezi kuti anawo azikhala aukhondo. Yehova nayenso amafuna kuti tizikhala aukhondo. (Eks. 30:18-20; Deut. 23:14; 2 Akor. 7:1) Timasonyeza kuti timalemekeza Yehova tikamasamalira thupi komanso zinthu zathu. (1 Pet. 1:14-16) Koma nanga bwanji nkhani yosamalira pakhomo pathu komanso malo ena? Anthu ambiri amangotaya zinyalala paliponse koma Akhristufe timafunika kuonetsetsa kuti dzikoli, lomwe ndi malo athu okhala, ndi laukhondo. (Sal. 115:16; Chiv. 11:18) Zinthu zina zomwe zimaoneka ngati nkhani yaing’ono monga kutaya paliponse zitsipe zanzimbe, makoko achimanga kapena anthochi, mapepala amaswiti komanso mabotolo azakumwa, kungasonyeze kuti si ife anthu aukhondo. Choncho tiyenera kusonyeza m’mbali zonse za moyo wathu “kuti ndife atumiki a Mulungu.”​—2 Akor. 6:3, 4.

ONERANI VIDIYO YAKUTI MULUNGU AMAKONDA ANTHU AUKHONDO KENAKO YANKHANI MAFUNSO OTSATIRAWA:

  • Kodi anthu ena amapereka zifukwa zotani akamalephera kusamalira zinthu zawo kuti zikhale zaukhondo?

  • Kodi Chilamulo cha Mose chinasonyeza bwanji kuti Yehova amafuna kuti anthu ake azikhala aukhondo?

  • Kodi tikamakhala aukhondo, timathandiza bwanji anthu ena kuti azilemekeza Yehova?

Bambo akulowa m’galimoto ya mwana wake yomwe ndi yakuda kwambiri; bambo ndi mwana wake akukambirana mfundo za Yehova za kufunika kokhala oyera; ansembe a m’nthawi ya Aisiraeli aima pafupi ndi beseni losambiramo lamkuwa; kagulu ka utumiki kakutuluka m’galimoto ya m’bale wachinyamata. Galimotoyo ikuoneka yaukhondo tsopano

Kodi ndingasonyeze bwanji kuti ndimaona ukhondo kukhala wofunika kwambiri ngati mmene Yehova amachitira?

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena