Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb19 December tsamba 8
  • Dziko “Linameza Mtsinje”

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Dziko “Linameza Mtsinje”
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2019
  • Nkhani Yofanana
  • Lipoti la Milandu
    Buku Lapachaka la Mboni za Yehova 2014
  • Olalikira Ufumu Anayamba Kupititsa Milandu Yawo Kukhoti
    Ufumu wa Mulungu Ukulamulira
  • Tisamaiwale Kupempherera Akhristu Amene Akuzunzidwa
    Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2017
  • Ufumu wa Mulungu Wabadwa
    Mapeto Osangalatsa a Masomphenya a M’buku la Chivumbulutso
Onani Zambiri
Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2019
mwb19 December tsamba 8
Zikalata za malamulo za bungwe la United Nations zofotokoza za kumangidwa kwa Mboni za Yehova ku Korea, zaikidwa pachithunzi cha abale a ku Korea omwe avala mayunifomu a kundende

MOYO WATHU WACHIKHRISTU

Dziko “Linameza Mtsinje”

Kuyambira kale, olamulira a dziko akhala akuthandiza anthu a Yehova. (Ezara 6:1-12; Esitere 8:10-13) Ngakhale masiku ano “dziko,” lomwe likuimira anthu a maganizo oyenera omwe ali ndi mphamvu m’dzikoli, limameza “mtsinje” wamavuto amene “njoka,” yomwe ndi Satana Mdyerekezi, amabweretsera atumiki a Yehova. (Chiv. 12:16) Yehova, yemwe ndi “Mulungu amene amatipulumutsa,” amatha kugwiritsa ntchito olamulira a dzikoli kuti athandize anthu ake.​—Sal. 68:20; Miy. 21:1.

Nanga bwanji ngati munamangidwa chifukwa cha zimene mumakhulupirira? Musakayikire kuti Yehova akuona zimene zikukuchitikirani. (Gen. 39:21-23; Sal. 105:17-20) Musamakayikirenso kuti Yehova adzakudalitsani kwambiri komanso musamaiwale kuti kukhulupirika kwanu kumalimbikitsa abale ndi alongo padziko lonse.​—Afil. 1:12-14; Chiv. 2:10.

ONERANI VIDIYO YAKUTI ABALE A KU KOREA ATULUTSIDWA M’NDENDE, KENAKO YANKHANI MAFUNSO OTSATIRAWA:

  • N’chifukwa chiyani abale ambiri a ku South Korea ankamangidwa?

  • Kodi khoti linagamula zotani kuti abale athu atulutsidwe m’ndende?

  • Kodi tingathandize bwanji abale athu padziko lonse omwe ali m’ndende chifukwa cha chikhulupiriro chawo?

  • Kodi tiyenera kugwiritsa ntchito bwanji ufulu umene tili nawo panopa?

  • Kodi ndi ndani amene amatithandiza kuti tipambane milandu yosiyanasiyana?

Ndende ya ku Korea yomwe munali a Mboni za Yehova; makalata amene a Mboni za Yehova anatumiza ku ofesi ya nthambi ya ku Korea omwe kenako anatumizidwa kwa abale amene anali m’ndende; bambo wakumbatirana ndi mwana wake yemwe watulutsidwa m’ndende

Kodi ndimagwiritsa ntchito bwanji ufulu umene ndili nawo panopa?

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena