Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb20 July tsamba 7
  • Yehova Amateteza Anthu Ake

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Yehova Amateteza Anthu Ake
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2020
  • Nkhani Yofanana
  • Chikhulupiriro Cholimba M’kati mwa Mavuto
    Galamukani!—2000
  • Kodi Ntchito Yomanga Ikuyenda Bwanji ku Warwick?
    Buku Lapachaka la Mboni za Yehova la 2016
  • Kodi Baibulo Limanena Zotani?
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawira)—2016
  • Zimene Zachitika M’chaka Chapitachi
    Buku Lapachaka la Mboni za Yehova la 2017
Onani Zambiri
Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2020
mwb20 July tsamba 7

MOYO WATHU WACHIKHRISTU

Yehova Amateteza Anthu Ake

Bambo wa Chiisiraeli ndi mwana wake akuwaza magazi pa mafelemu a nyumba yawo.

Chikondwerero cha Pasika woyamba chinali chofunika kwambiri. Usiku umenewo, Farao ataona kuti mwana wake woyamba kubadwa wafa, anauza Mose kuti: “Nyamukani, chokani pakati pa anthu anga, inuyo ndi ana onse a Isiraeli. Pitani, katumikireni Yehova, monga momwe mwanenera.” (Eks 12:31) Pa nthawiyi Yehova anasonyeza kuti amateteza anthu ake.

Tikaganizira mbiri ya atumiki a Yehova a masiku ano, n’zoonekeratu kuti Yehova akupitiriza kutsogolera komanso kuteteza anthu ake. Zimenezi zinafotokozedwa bwino kumalo osungirako zinthu zakale otchedwa “Anthu Odziwika ndi Dzina la Yehova” omwe ali kulikulu la padziko.

ONERANI VIDIYO YAKUTI KUONA MALO OSUNGIRAKO ZINTHU ZAKALE KU WARWICK: “ANTHU ODZIWIKA NDI DZINA LA YEHOVA,” NDIPO KENAKO YANKHANI MAFUNSO OTSATIRAWA:

  • Zithunzi za mu ‘Sewero la Pakanema la Chilengedwe.’

    Kuyambira mu 1914, kodi Ophunzira Baibulo anayamba kugwiritsa ntchito njira yatsopano iti pofuna kuthandiza anthu kuti azikhulupirira Baibulo, nanga njirayi inathandiza bwanji?

  • Zinthuzi za abale omwe anaikidwa m’ndende mu 1918.

    Kodi Ophunzira Baibulo anakumana ndi mayesero otani mu 1916 ndi 1918, nanga panali umboni wotani wosonyeza kuti Yehova ankatsogolera gulu lake?

  • Chithunzi chomwe chili ku malo osungirako zinthu zakale chosonyeza abale omwe anamangidwa chifukwa cha chikhulupiriro chawo. Khomo lotsegula lolowera kuchipinda komwe kuli zithunzi zosonyeza Paradaiso.

    Kodi n’chiyani chinathandiza anthu a Yehova kukhalabe okhulupirika ngakhale kuti ankatsutsidwa?

  • Zithunzi zomwe zili ku malo osungirako zinthu zakale zosonyeza njira zolalikirira zomwe zinkagwiritsidwa ntchito m’ma 1930 ndi m’ma 1940.

    Kodi ndi mfundo yatsopano iti imene anthu a Yehova anauzidwa mu 1935, nanga zimenezi zinawakhudza bwanji?

  • Ngati munakaona malo osungira zinthu zakale amenewa, kodi n’chiyani chinakutsimikizirani kuti Yehova akutsogolera komanso kuteteza anthu ake?

Ngati mukufuna kudziwa zimene mungachite kuti mukaone malo osungirako zinthu zakalewa, pitani pa jw.org® ndipo dinani pomwe alemba kuti Zokhudza Ifeyo

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena