Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb22 September tsamba 13
  • Zinthu Zothandiza Zomwe Zili M’buku Lakuti “Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale”

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zinthu Zothandiza Zomwe Zili M’buku Lakuti “Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale”
  • Kabuku ka Msonkhano wa Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—2022
  • Nkhani Yofanana
  • Muzigwiritsa Ntchito Mavidiyo Pophunzira ndi Anthu
    Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2019
  • Magazini Yophunzira Yatsopano ya Nsanja ya Olonda
    Nsanja ya Olonda—2008
  • Musamagwiritse Ntchito Zipangizo Zamakono Monyanyira
    Galamukani!—2015
  • Zimene Zasintha M’magazini Yophunzira
    Nsanja ya Olonda—2012
Onani Zambiri
Kabuku ka Msonkhano wa Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—2022
mwb22 September tsamba 13

MOYO WATHU WACHIKHRISTU

Zinthu Zothandiza Zomwe Zili M’buku Lakuti Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale

Kodi mumakonda kugwiritsa ntchito mavidiyo komanso mafunso a m’buku la Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale omwe amathandiza munthu kufotokoza maganizo ake? Nanga bwanji mbali zina ngati “Zimene Ena Amanena,” “Zolinga” komanso “Onani Zinanso”? Ndi zinthu zinanso ziti zimene mumaona kuti zimakuthandizani mukamagwira ntchito yophunzitsa anthu?​—Mt 28:19, 20.

Buku la “Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale” lili pa “JW Library.” Asonyeza pamene pali batani la “Mavidiyo ndi Zinthu Zina za mu Gawo 1.”

Mavidiyo ndi Zinthu Zina: Ngati mumakonda kugwiritsa ntchito buku losindikizidwa pochititsa phunziro la Baibulo, kodi mungatani kuti mupeze mavidiyo ndi zinthu zina zonse pamalo amodzi? M’buku la pazipangizo zamakono sankhani chigawo chimodzi pa zigawo 4 zomwe zili m’bukuli. Pansi penipeni pa mitu ya maphunziro, mukhoza kupeza mavidiyo komanso zinthu zina zimene zili m’chigawocho. (Onani chithunzi 1)

Batani la “Printed Edition”: Ngati mukuphunzira ndi munthu pogwiritsa ntchito buku la pachipangizo chamakono, mwina nthawi zina pa nthawi ya phunzirolo mungakonde kuona la “Printed Edition.” Mukatsegula phunzirolo dinani timadontho titatu tomwe tili pamwamba mbali ya kumanja kenako dinani pamene alemba kuti “Printed Edition.” Zikatero tsamba lonse limaoneka pa sikirini ndipo zimakuthandizani kuti mugwirizanitse mfundo zonse za mu phunzirolo mosavuta. Kuti mubwerere ku buku la pachipangizo chamakono dinaninso timadontho titatu tija ndipo pitani pa “Digital Edition.”

Buku la “Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale” lili pa “JW Library.” Asonyeza pamene pali bokosi akuti “Kodi Ndakonzeka?” komanso “Mawu Akumapeto.”

“Kodi Ndakonzeka?”: Mabokosi awiri amenewa omwe ali chakumapeto kwa bukuli, ali ndi mfundo zomwe zingathandize wophunzira kudziwa ngati ali woyenerera kuyamba kulalikira limodzi ndi mpingo komanso kubatizidwa. (Onani chithunzi 2.)

Mawu Akumapeto: Mawu akumapeto amafotokozera mfundo zikuluzikulu zomwe zili m’bukuli. M’buku la pachipangizo chamakono, kumapeto kwa mawu akumapeto alionse, kumakhala linki yomwe imakutengeraninso ku phunziro limene munapezako mawu akumapetowo. (Onani chithunzi 2.)

Muzionetsetsa kuti mwamaliza kuphunzira buku la Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale ngakhale wophunzirayo atabatizidwa. Muziperekerabe lipoti phunzirolo, nthawi komanso maulendo obwereza ngakhale pambuyo poti wophunzirayo wabatizidwa. Ngati mwapita ku phunziroko ndi wofalitsa wina ndipo nayenso anaphunzitsa nawo, aziwerengera nthawi

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena