Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb23 January tsamba 9
  • Yehova Amatithandiza Tikamakumana ndi Mayesero

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Yehova Amatithandiza Tikamakumana ndi Mayesero
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—2023
  • Nkhani Yofanana
  • Muzikumbukira Yehova Yemwe ndi “Mulungu Wamoyo”
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2024
  • Mafunso Ochokera kwa Owerenga
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2017
  • Sitili Tokha
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2025
  • Kodi Mayesero Tiziwaona Bwanji?
    Nsanja ya Olonda—2002
Onani Zambiri
Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—2023
mwb23 January tsamba 9
Makolo ndi ana awo awiri akuchita misonkhano ndi mpingo wawo kudzera pa vidiyokomfelensi.

MOYO WATHU WACHIKHRISTU

Yehova Amatithandiza Tikamakumana ndi Mayesero

M’masiku otsiriza ano, tikukumana ndi mayesero osiyanasiyana. Nthawi zina, timaona kuti mayesero ena amakhala ovuta kwambiri kuwapirira. Komabe ngati titapitiriza kukhala pa ubwenzi wabwino ndi Yehova, iye akhoza kutithandiza kupirira ngakhale mayesero ovuta kwambiriwo. (Yes 43:2, 4) Ndiye kodi tingatani kuti tikhalebe pa ubwenzi wabwino ndi Yehova pamene tikukumana ndi mayesero?

Pemphero. Tikamuuza Yehova zamumtima mwathu, iye amatipatsa mtendere komanso mphamvu kuti tipirire.​—Afi 4:6, 7; 1At 5:17.

Misonkhano. Kuposa kale lonse, panopa tikufunika chakudya chauzimu chimene Yehova amatipatsa komanso kusonkhana limodzi ndi abale athu. (Ahe 10:24, 25) Tikamakonzekera, kupezeka komanso kuyankha pa misonkhano, mzimu wa Yehova umatithandiza kwambiri.​—Chv 2:29.

Kulalikira. Zimakhala zosavuta kuganizira zinthu zabwino ngati timachita zonse zomwe tingathe kuti tizichita zambiri mu utumiki. Timalimbitsanso ubwenzi wathu ndi Yehova komanso Akhristu anzathu.​—1Ak 3:5-10.

ONERANI VIDIYO YAKUTI YEHOVA ADZAKHALA NAWE, KENAKO YANKHANI MAFUNSO OSATIRAWA:

  • Kodi n’chiyani chinathandiza Malu kuti akhalebe pa ubwenzi wabwino ndi Yehova pamene ankakumana ndi mayesero?

  • Mofanana ndi Malu, kodi mawu opezeka pa Salimo 34:18 angatilimbikitse bwanji pamene tikukumana ndi mayesero?

  • Kodi zomwe zinachitikira Malu zikusonyeza bwanji kuti Yehova amatipatsa “mphamvu yoposa yachibadwa” tikamakumana ndi mayesero?​—2Ak 4:7.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena