Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w24 September tsamba 32
  • Muzikhala Okonzeka Kuphunzira Zinthu Zatsopano

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Muzikhala Okonzeka Kuphunzira Zinthu Zatsopano
  • Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2024
  • Nkhani Yofanana
  • Yehova Amasamalira Anthu Ake
    Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2017
  • Kodi Zinthu Zonse Zimene Yehova Amatipatsa Zimakuthandizani?
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2016
  • Kuphunzira Kumapindulitsa
    Pindulani ndi Sukulu ya Utumiki wa Mulungu
  • Tsanzirani Chitsanzo cha Mfumu
    Nsanja ya Olonda—2002
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2024
w24 September tsamba 32

MFUNDO ZOTHANDIZA POPHUNZIRA

Muzikhala Okonzeka Kuphunzira Zinthu Zatsopano

Mukamakonzekera kuphunzira mungadzifunse kuti, ‘Kodi ndikuyembekezera kuphunzirapo chiyani?’ Ngakhale kuti mungadziwiretu zimene muphunzire, muzikumbukira kuti pangakhalenso zinthu zina zatsopano zimene Yehova angakuphunzitseni. Ndiye kodi mungatani kuti muzikhala okonzeka kuphunzira zinthu zatsopano?

Muzipempha nzeru. Muzipempha Yehova kuti akuthandizeni kumvetsa zimene akufuna kuti muphunzire panopa. (Yak. 1:5) Musamangokhutira ndi zimene munadziwa kale.—Miy. 3:​5, 6.

Muzikumbukira kuti Baibulo ndi lamphamvu. “Mawu a Mulungu ndi amoyo.” (Aheb. 4:12) “Mawu” a Mulungu omwe ndi amoyo angatithandize m’njira zosiyanasiyana nthawi iliyonse imene tikuwawerenga. Komatu izi zingatheke ngati tili okonzeka kuphunzira zinthu zatsopano pa zimene tikuwerengazo.

Muziyamikira zilizonse zomwe Yehova amakuphunzitsani. Chakudya chauzimu chili ngati “phwando la zakudya zabwino kwambiri.” (Yes. 25:6) Choncho muzipewa kusala “zakudya” zimene mumaona kuti sizikusangalatsani. Kuchita zimenezi kudzakuthandizani kuti mukhale munthu wabwino komanso muzisangalala kwambiri mukamaphunzira.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena