Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • wp25 No. 1 tsamba 9
  • N’chifukwa Chiyani Nkhondo Komanso Zachiwawa Zikuchitikabe Padzikoli?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • N’chifukwa Chiyani Nkhondo Komanso Zachiwawa Zikuchitikabe Padzikoli?
  • Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawira)—2025
  • Timitu
  • Nkhani Yofanana
  • UCHIMO
  • MABOMA A ANTHU
  • SATANA NDI ZIWANDA ZAKE
  • Kodi Nkhondo Komanso Zachiwawa Zidzathetsedwa Bwanji?
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawira)—2025
  • Kodi Mulungu Analenga Anthu Chifukwa Chiyani?
    Zimene Baibulo Limaphunzitsa
  • Kodi Tchimo Loyambirira Linali Chiyani?
    Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
  • Kodi Nkhondo Komanso Zachiwawa Zimatikhudza Bwanji Tonsefe?
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawira)—2025
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawira)—2025
wp25 No. 1 tsamba 9

N’chifukwa Chiyani Nkhondo Komanso Zachiwawa Zikuchitikabe Padzikoli?

Baibulo limafotokoza zinthu zimene zimachititsa kuti nkhondo komanso zachiwawa zizipitirira padzikoli.

UCHIMO

Mulungu analenga makolo athu oyamba, Adamu ndi Hava, m’chifaniziro chake. (Genesis 1:27) Zimenezi zikutanthauza kuti mwachibadwa, anthuwa ankafunika kusonyeza makhalidwe a Mulungu monga mtendere komanso chikondi. (1 Akorinto 14:33; 1 Yohane 4:8) Komabe, Adamu ndi Hava sanamvere Mulungu ndipo anachimwa. Chifukwa cha zimenezi, tonsefe tinatengera uchimo ndi imfa. (Aroma 5:12) Choncho, popeza kuti tinatengera uchimowu, tonsefe timakhala ndi maganizo ofuna kuchita zachiwawa.—Genesis 6:5; Maliko 7:21, 22.

MABOMA A ANTHU

Mulungu sanatilenge kuti tizidzilamulira. Baibulo limanena kuti: “Munthu amene akuyenda alibe ulamuliro wowongolera mapazi ake.” (Yeremiya 10:23) N’chifukwa chake n’zosatheka kuti maboma a anthu athetseretu nkhondo ndiponso zachiwawa.

SATANA NDI ZIWANDA ZAKE

Baibulo limanena kuti “dziko lonse lili mʼmanja mwa woipayo.” (1 Yohane 5:19) “Woipayo” amene akutchulidwa pavesili ndi Satana Mdyerekezi ndipo iye ndi chigawenga chopha anthu. (Yohane 8:44) Ngakhale kuti Satana ndi ziwanda zake saoneka, iwo ndi amene amachititsa kuti anthu azimenya nkhondo komanso azichita zachiwawa.—Chivumbulutso 12:9, 12.

Anthu sangakwanitse kuthetsa zimene zimayambitsa nkhondo komanso zachiwawa koma Mulungu ndi amene angazithetse

Chipembedzo Komanso Nkhondo

Kawirikawiri, zipembedzo zimalekerera, kuvomereza komanso kulimbikitsa nkhondo. Zimenezi ndi zipembedzo zabodza zimene Baibulo limazitchula kuti “Babulo Wamkulu.” (Chivumbulutso 18:2) Mulungu amanena kuti Babulo Wamkulu ali ndi mlandu wopha anthu “onse amene anaphedwa padziko lapansi.” (Chivumbulutso 18:24) Kuti mudziwe zambiri werengani nkhani yakuti “Kodi Babulo Wamkulu N’chiyani?” pa jw.org.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena