Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • yb14 tsamba 169
  • Ndinayamba Kulikonda Kwambiri Dziko la Sierra Leone

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Ndinayamba Kulikonda Kwambiri Dziko la Sierra Leone
  • Buku Lapachaka la Mboni za Yehova 2014
  • Nkhani Yofanana
  • Ntchito Yopanga Ophunzira Yakhudza Kwambiri Zochita Pamoyo Wanga
    Nsanja ya Olonda—2007
  • Tinkafunitsitsa Kutumikira Yehova
    Buku Lapachaka la Mboni za Yehova 2014
  • Ndinapeza Chinthu Chamtengo Wapatali Kuposa Dayamondi
    Buku Lapachaka la Mboni za Yehova 2014
  • Ndimakhala Wosatekeseka Chifukwa Chodalira Yehova
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2023
Onani Zambiri
Buku Lapachaka la Mboni za Yehova 2014
yb14 tsamba 169

SIERRA LEONE AND GUINEA

Ndinayamba Kulikonda Kwambiri Dziko la Sierra Leone

Cindy McIntire

  • CHAKA CHOBADWA 1960

  • CHAKA CHOBATIZIDWA 1974

  • MBIRI YAKE Anayamba umishonale mu 1992. Watumikira ku Guinea ndi ku Senegal. Panopa akutumikira ku Sierra Leone.

NDITANGOKHALA milungu iwiri yokha ku Sierra Leone ndinayamba kulikonda kwambiri dzikoli. Ndinkachita chidwi ndikaona anthu atadendekera katundu wolemera. M’madera osiyanasiyana munkangokhala anthu balalabalala. Ana ankakonda kusewera komanso kuvina mumsewu kwinaku akuwomba m’manja. Ndinkachita chidwi ndi zimene anthu ankachita komanso nyimbo zawo.

Koma chimene chimandisangalatsa kwambiri kunoko ndi kulalikira. Anthu a ku Sierra Leone amalandira bwino alendo. Amalemekeza Baibulo ndipo amamvetsera kwambiri. Nthawi zambiri amandiitanira m’nyumba zawo. Ndikamachoka, ena amandiperekeza mpaka kukandifikitsa kumsewu. Zimenezi zimandithandiza kuti ndizipirira mavuto ang’onoang’ono amene ndimakumana nawo monga kusowa kwa madzi komanso magetsi.

Chifukwa chakuti sindili pabanja, nthawi zina anthu amandifunsa ngati ndimasowa wocheza naye. Koma zoona zake n’zakuti, ndimakhala ndi zochita zambiri moti sindikhala ndi nthawi yomaonanso ngati ndilibe wocheza naye. Ndine wosangalala chifukwa ndimakhala ndi zochita zambiri.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena