Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mrt nkhani 107
  • Yesu Adzathetsa Nkhondo

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Yesu Adzathetsa Nkhondo
  • Nkhani Zina
  • Nkhani Yofanana
  • Yesu Adzathetsa Umphawi
    Nkhani Zina
  • Ndi Ndani Angateteze Anthu Wamba Pankhondo?—Kodi Baibulo Limanena Zotani?
    Nkhani Zina
  • N’chifukwa Chiyani Ndale Zimagawanitsa Kwambiri Anthu?—Kodi Baibulo Limanena Zotani?
    Nkhani Zina
  • Yesu Ankaona Kuti Ufumu wa Mulungu Ndi Wofunika Kwambiri
    Nsanja ya Olonda—2014
Onani Zambiri
Nkhani Zina
mrt nkhani 107
Anyamata awiri akhala pansi, akuyang’ana mmene nkhondo yawonongera zinthu.

AspctStyle/stock.adobe.com

Yesu Adzathetsa Nkhondo

Ali padzikoli, Yesu anasonyeza chikondi chachikulu kwa anthu onse, moti anafika popereka moyo wake kuti awawombole. (Mateyu 20:28; Yohane 15:13) Posachedwapa, adzasonyeza umboni winanso wakuti amakonda anthu onse pogwiritsa ntchito mphamvu zake monga Mfumu ya Ufumu wa Mulungu. Iye ‘adzathetsa nkhondo padziko lonse lapansi.’—Salimo 46:9.

Taonani zimene Baibulo limanena zokhudza zimene Yesu adzachite:

  • “Adzapulumutsa wosauka amene akufuula popempha thandizo, komanso wonyozeka ndi aliyense amene alibe womuthandiza. Adzamvera chisoni munthu wonyozeka ndi wosauka, ndipo adzapulumutsa miyoyo ya anthu osauka. Adzawapulumutsa kuti asaponderezedwe komanso kuchitiridwa zachiwawa.”—Salimo 72:12-14.

Kodi tingasonyeze bwanji kuti timayamikira zonse zimene Yesu anatichitira komanso zimene atichitire posachedwapa?. Njira imodzi ndi kuphunzira zokhudza “uthenga wabwino wa Ufumu wa Mulungu” umene ankalalikira. (Luka 4:43) Werengani nkhani yakuti “Kodi Ufumu wa Mulungu N’chiyani?”

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena