Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mrt nkhani 108
  • Yesu Adzathetsa Umphawi

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Yesu Adzathetsa Umphawi
  • Nkhani Zina
  • Nkhani Yofanana
  • Yesu Adzathetsa Nkhondo
    Nkhani Zina
  • Tsanzirani Yesu Poganizira Osauka
    Nsanja ya Olonda—2006
  • Yesu Adzathetsa Zoipa Zonse
    Nkhani Zina
  • Kodi Mungakhulupirire Ndani?—Zimene Baibulo Limanena?
    Nkhani Zina
Onani Zambiri
Nkhani Zina
mrt nkhani 108
Munthu watambasula manja ake pamene akupempha.

panitan/stock.adobe.com

Yesu Adzathetsa Umphawi

Ali padzikoli, Yesu anasonyeza chikondi chachikulu kwa anthu, makamaka osauka komanso amene anali ndi nkhawa. (Mateyu 9:36) Iye anafika popereka moyo wake kuti athandize anthu. (Mateyu 20:28; Yohane 15:13) Posachedwapa, asonyezanso kuti amakonda kwambiri anthu pamene athetse umphawi padziko lonse pogwiritsa ntchito mphamvu komanso udindo wake monga Mfumu ya Ufumu wa Mulungu.

Baibulo limafotokoza mwandakatulo zimene Yesu adzachite, limati:

  • “Ateteze anthu onyozeka pakati pa anthu, apulumutse ana a anthu osauka.”—Salimo 72:4.

Kodi tingasonyeze bwanji kuti timayamikira zonse zimene Yesu anatichitira komanso zimene atichitire posachedwapa? Njira imodzi imene tingachitire zimenezi ndi kuphunzira zambiri zokhudza “uthenga wabwino wa Ufumu wa Mulungu” umene iye ankalalikira. (Luka 4:43) Werengani nkhani yakuti “Kodi Ufumu wa Mulungu N’chiyani?”

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena