Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mrt nkhani 109
  • Yesu Adzathetsa Zoipa Zonse

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Yesu Adzathetsa Zoipa Zonse
  • Nkhani Zina
  • Nkhani Yofanana
  • Yesu Adzathetsa Umphawi
    Nkhani Zina
  • Yesu Adzathetsa Nkhondo
    Nkhani Zina
  • Kodi Mungakhulupirire Ndani?—Zimene Baibulo Limanena?
    Nkhani Zina
  • Mapeto a Upandu Ali Pafupi Tsopano!
    Nsanja ya Olonda—1989
Onani Zambiri
Nkhani Zina
mrt nkhani 109
Chigawenga chikuzemberera mzimayi yemwe ali yekhayekha. Iye waona chigawengacho kumbuyo kwake ndipo akuimbira foni anthu kuti amuthandize.

alfa27/stock.adobe.com

Yesu Adzathetsa Zoipa Zonse

Yesu amadziwa bwino mmene munthu amamvera akamavutika chifukwa cha uchigawenga ndi zinthu zopanda chilungamo. Iye anaimbidwa mlandu wabodza, anamenyedwa ngakhale kuti sanalakwe, anaweruzidwa mopanda chilungamo komanso anafa imfa yowawa kwambiri. Yesu anali wosalakwa koma mofunitsitsa anapereka “moyo wake dipo kuti awombole anthu ambiri.” (Mateyu 20:28; Yohane 15:13) Monga Mfumu ya Ufumu wa Mulungu, posachedwapa Yesu abweretsa chilungamo padziko lonse ndipo athetseratu zoipa zonse.—Yesaya 42:3.

Baibulo limafotokoza zimene zidzachitike padzikoli Yesu akadzayamba kulamulira:

  • “Oipa sadzakhalaponso. Udzayangʼana pamene ankakhala, ndipo sadzapezekapo. Koma anthu ofatsa adzalandira dziko lapansi, ndipo adzasangalala ndi mtendere wochuluka.”—Salimo 37:10, 11.

Kodi tingasonyeze bwanji kuti timayamikira zonse zimene Yesu anatichitira komanso zimene atichitire posachedwapa? Njira imodzi imene tingachitire zimenezi ndi kuphunzira zambiri zokhudza “uthenga wabwino wa Ufumu wa Mulungu” umene iye ankalalikira. (Luka 4:43) Werengani nkhani yakuti “Kodi Ufumu wa Mulungu N’chiyani?”

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena