Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • ijwfq nkhani 26
  • Kodi Muli ndi Amishonale?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Muli ndi Amishonale?
  • Mafunso Ofunsidwa Kawirikawiri
  • Nkhani Yofanana
  • “Dzanja la Yehova Linali Nawo”
    Nsanja ya Olonda—1989
  • Kuphunzitsa Atumiki a Ufumu
    Ufumu wa Mulungu Ukulamulira
  • Nyumba Yatsopano Kaamba ka Sukulu ya Mishonale ya Gileadi
    Nsanja ya Olonda—1989
  • Kodi Apainiya Ali Ndi Mwayi Wochita Maphunziro Otani?
    Kodi Ndani Akuchita Chifuniro cha Yehova Masiku Ano?
Onani Zambiri
Mafunso Ofunsidwa Kawirikawiri
ijwfq nkhani 26

Kodi a Mboni za Yehova Ali ndi Amishonale?

Inde. Kulikonse kumene tili, anthu tonse a Mboni za Yehova timayesetsa kukhala ndi mtima waumishonale, kutanthauza kuti nthawi zonse timayesetsa kuuza ena zimene timakhulupirira.—Mateyu 28:19, 20.

Kuwonjezera pamenepa, anthu ena a Mboni nthawi zambiri amapita kapena kusamukira m’madera ena a m’dziko lawo lomwelo, kumene anthu ambiri sanamvepo uthenga wabwino wa m’Baibulo. Koma a Mboni ena amasamukira m’mayiko ena n’cholinga choti azikalalikira uthenga wabwino. Iwo amasangalala kuchita zimenezi chifukwa amathandiza pokwaniritsa ulosi umene Yesu ananena kuti: “Mudzakhala mboni zanga . . . mpaka kumalekezero a dziko lapansi.”—Machitidwe 1:8.

Mu 1943, tinatsegula sukulu yophunzitsa anthu ntchito ya umishonale. Kuyambira m’chaka chimenecho, anthu a Mboni oposa 8,000 aphunzitsidwa kusukulu imeneyi, yomwe imadziwika ndi dzina lakuti Sukulu ya Giliyadi Yophunzitsa Baibulo.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena