Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • ijwwd nkhani 4
  • Khungu la Nangumi Lotha Kudziyeretsa Lokha

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Khungu la Nangumi Lotha Kudziyeretsa Lokha
  • Kodi Zinangochitika Zokha?
  • Nkhani Yofanana
  • Nyama Zikuluzikulu za M’nyanja
    Galamukani!—2009
  • Guluu wa Kanyama Kotchedwa Barnacle
    Kodi Zinangochitika Zokha?
  • Kodi Munazionapo Zinsomba Zikuluzikulu Izi?
    Galamukani!—2015
  • Zipsepse za Nangumi
    Galamukani!—2013
Onani Zambiri
Kodi Zinangochitika Zokha?
ijwwd nkhani 4
Nangumi

KODI ZINANGOCHITIKA ZOKHA?

Khungu la Nangumi Lotha Kudziyeretsa Lokha

Tizilombo tinatake komanso zomera zimene zimakakamira kumimba kwa sitima za m’madzi, zimachititsa kuti kuyendetsa sitimazo kukhale kovuta. Zamoyo zimenezi zimapangitsa kuti sitima ziziwononga mafuta ambiri, zizikanika kuyenda mofulumira, komanso zimachititsa kuti pambuyo pa zaka zingapo zilizonse, azisiya kaye kuzigwiritsa ntchito mpaka atazipala kuti ziyere. Panopa asayansi ayamba kufufuza m’zinthu zachilengedwe kuti apeze njira yothetsera vutoli.

Taganizirani izi: Ochita kafukufuku anapeza kuti khungu la nangumi wotchedwa pilot whale (Globicephala melas) limatha kudziyeretsa lokha. Khunguli lili ndi timizere ting’onoting’ono kwambiri ndipo zimenezi zimachititsa kuti mazira a tizilomboti azikanika kumatilira. Pakati pa timizereti pamakhala mafuta enaake amene amalimbana ndi ndere komanso mabakiteriya. Nangumi akafundula, thupi lake limatulutsa mafuta ena oteteza khungu lake.

Asayansi akufuna kutengera luso lomatha kudziyeretsali popanga zinthu zotetezera sitima za m’madzi. Poyamba ankapaka sitimazi penti woteteza kuti tizilombo tisamamatilire. Koma posachedwapa aletsa kugwiritsa ntchito mitundu ya penti imene anthu ankakonda kugwiritsa ntchito chifukwa imawononga zamoyo za m’madzi. Ochita kafukufuku akuganiza zoti aziika mawaya kuzungulira sitimazi ndipo mkati mwake muzikhala timabowo tomwe tizitulutsa mankhwala osawononga zachilengedwe. Mankhwalawo akangogundana ndi madzi, azilimba n’kukhala aphalaphala ndipo azikuta kumimba konse kwa sitimayo. Pakapita nthawi, ziphalaphala zimenezi zizichoka ndipo zizichokera limodzi ndi zamoyo zonse zomwe zinakakamira kusitimayo. Zimenezi zikangochitika, mankhwala ena azituluka n’kupanganso chiphalaphala china chokuta kumimba kwa sitimayo.

Tizilombo komanso zomera zakakamira kumimba kwa sitima

Zinthu zokakamira kusitima zimapangitsa kuti iziyenda movutikira komanso zimavuta kuchotsa

Akatswiri akhala akuyeserera njirayi ndipo zimene apeza n’zakuti ikhoza kuthandiza kuti pazidutsa nthawi yaitali kwambiri zamoyozi zisanachulukane kumimba kwa sitima. Zimenezi zingathandize kwambiri makampani a sitima za pamadzi chifukwa kubweretsa sitima kumtunda kuti aitsuke kumawononga ndalama zambiri.

Kodi inuyo mukuganiza bwanji? Kodi khungu la nangumi lomatha kudziyeretsa lokhali linangokhalapo lokha, kapena linalengedwa ndi winawake?

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena