19 Zikadzatero adzakukwezani pamwamba pa mitundu ina yonse imene anapanga.+ Zimenezi zidzachititsa kuti mutamandidwe, mutchuke komanso kuti mulandire ulemerero mukapitiriza kukhala anthu oyera kwa Yehova Mulungu wanu,+ mogwirizana ndi zimene anakulonjezani.”