17 Ndiyeno Davide anatuluka kukakumana nawo ndipo anawauza kuti: “Ngati mwabwerera mtendere komanso kudzandithandiza, mtima wanga ugwirizana nanu. Koma ngati mwabwera kudzandipereka kwa adani anga, pamene manja anga ndi osalakwa, Mulungu wa makolo athu aone zimenezo ndipo aweruze.”+