17 Asanamalize kulankhula, munthu winanso anabwera nʼkudzanena kuti: “Akasidi+ anapanga magulu atatu ndipo anaukira ngamila zanu nʼkuzitenga, komanso apha atumiki anu ndi lupanga. Ine ndekha ndi amene ndapulumuka, choncho ndabwera kudzakuuzani uthengawu.”