-
Yeremiya 24:1Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
24 Kenako Yehova anandionetsa madengu awiri a nkhuyu amene anali patsogolo pa kachisi wa Yehova. Anandionetsa madenguwo pambuyo poti Nebukadinezara* mfumu ya Babulo watenga Yekoniya*+ mwana wa Yehoyakimu,+ mfumu ya Yuda, pamodzi ndi akalonga a Yuda, amisiri komanso anthu osula zitsulo,* kuchoka ku Yerusalemu nʼkupita nawo ku ukapolo ku Babulo.+
-