11 Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, wanena kuti: ‘Ombani mʼmanja mowawidwa mtima ndipo pondani pansi posonyeza kuti muli ndi chisoni chachikulu. Mulire chifukwa cha zoipa zonse komanso zonyansa zimene Aisiraeli anachita chifukwa iwo adzaphedwa ndi lupanga, njala ndi mliri.+