9 “Yehova wa magulu ankhondo akumwamba wanena kuti, ‘Limbani mtima ndipo mukonzeke kugwira ntchito,+ inu amene mukumva mawu a aneneri+ masiku ano. Awa ndi mawu amene ananenedwanso tsiku limene maziko a nyumba ya Yehova wa magulu ankhondo akumwamba anayalidwa kuti kachisi amangidwe.