23 Ngakhale kuti zinthu zimenezo zimaoneka ngati zanzeru, amene amazichitawo amasankha okha njira yolambirira. Iwo amazunza thupi lawo+ kuti anthu aziona ngati ndi odzichepetsa. Koma zimenezo nʼzosathandiza kwa munthu amene akulimbana ndi zimene thupi limalakalaka.