13 Ndipo pa mwana wa nkhosa wamphongo aliyense, yomwe ndi nsembe yopsereza yafungo lokhazika mtima pansi,+ nsembe yotentha ndi moto yoperekedwa kwa Yehova, muziperekanso nsembe yambewu ya ufa wosalala wothira mafuta. Ufawo uzikhala wokwana gawo limodzi mwa magawo 10 a muyezo wa efa.