36 Pa tsikuli, muzipereka nsembe yopsereza yotentha ndi moto yafungo lokhazika mtima pansi kwa Yehova. Nsembeyo izikhala ya ng’ombe imodzi yamphongo, nkhosa imodzi yamphongo, ndi ana a nkhosa 7 amphongo, ndipo mwana wa nkhosa aliyense azikhala wachaka chimodzi, wopanda chilema.+