13 Ndipo adzakukondani ndithu, kukudalitsani,+ kukuchulukitsani+ ndi kudalitsa zipatso za mimba yanu+ ndi zipatso za nthaka yanu.+ Adzadalitsa mbewu zanu, vinyo wanu watsopano ndi mafuta anu, ana a ng’ombe zanu ndi ana a nkhosa zanu,+ m’dziko limene analumbirira makolo anu kuti adzakupatsani.+