7 Pamenepo Mose anaitana Yoswa ndi kumuuza pamaso pa Aisiraeli onse kuti: “Limba mtima ndipo uchite zinthu mwamphamvu,+ chifukwa ndiwe amene udzalowetsa anthu awa m’dziko limene Yehova analumbirira makolo awo kuti adzawapatsa.+ Ndipo iwe ndi amene udzawapatsa dzikolo monga cholowa chawo.