21 Choncho Zeba ndi Zalimuna anati: “Nyamuka iweyo utiphe wekha. Munthu amakhala ndi mphamvu+ zolingana ndi msinkhu wake.” Motero Gidiyoni ananyamuka ndi kupha+ Zeba ndi Zalimuna, ndipo anatenga zokongoletsa zooneka ngati mwezi zimene zinali pakhosi la ngamila zawo.