Loweruka, August 30
Tizitonthoza [ena] . . . chifukwa nafenso tatonthozedwa ndi Mulungu.—2 Akor. 1:4.
Yehova amatsitsimula komanso kutonthoza anthu omwe akumana ndi mavuto. Kodi tingatsanzire bwanji Yehova potonthoza ena komanso kusonyeza chifundo? Tingachite zimenezi poyesetsa kukhala ndi makhalidwe amene angatithandize kuti titonthoze anthu ena. Kodi ena mwa makhalidwe amenewa ndi ati? Nanga n’chiyani chingatithandize kukhala ndi chikondi chimene chimafunika kuti tizitonthozana kapena kuti “kulimbikitsana” tsiku ndi tsiku? (1 Ates. 4:18) Tiyenera kukhala ndi makhalidwe monga kumvera ena chisoni, kukonda abale komanso kukoma mtima. (Akol. 3:12; 1 Pet. 3:8) Kodi makhalidwe amenewa angatithandize bwanji? Tikamakhala ndi chifundo komanso makhalidwe amene tatchulawa, sitingachitire mwina koma kutonthoza ena. Paja Yesu anati: “Pakamwa pamalankhula zosefukira mumtima. Munthu wabwino amatulutsa zabwino m’chuma chabwino chamumtima mwake, koma munthu woipa amatulutsa zoipa m’chuma choipa chamumtima mwake.” (Mat. 12:34, 35) Kutonthoza abale ndi alongo athu omwe akumana ndi mavuto ndi njira yofunika kwambiri yomwe tingasonyezere kuti timawakonda. w23.11 10 ¶10-11
Lamlungu, August 31
Anthu ozindikira adzawamvetsetsa.—Dan. 12:10.
Tiyenera kupempha Mulungu kuti atithandize kumvetsa ulosi wa m’Baibulo. Taganizirani chitsanzo ichi: Tayerekezerani kuti mukuyenda m’dera lachilendo koma mnzanu amene mwayenda naye akudziwa bwino deralo. Akudziwa bwino pamene muli komanso kumene msewu uliwonse ukulowera. Mosakayikira mungasangalale kuti mnzanuyo anavomera kuti muyende naye. Mofanana ndi zimenezi, Yehova akudziwa bwino nthawi yomwe tikukhalamoyi komanso zimene zichitike kutsogoloku. Choncho kuti tizimvetsa maulosi a m’Baibulo, modzichepetsa tiyenera kupempha Yehova kuti atithandize. (Dan. 2:28; 2 Pet. 1:19, 20) Mofanana ndi kholo lililonse lachikondi, Yehova amafuna kuti ana ake akhale ndi tsogolo labwino. (Yer. 29:11) Koma mosiyana ndi makolo athu, Yehova akhoza kuneneratu zinthu zimene zidzachitike m’tsogolo molondola kwambiri. Iye analola kuti maulosi alembedwe m’Mawu ake ndi cholinga choti tizidziwa zinthu zofunika zisanachitike.—Yes. 46:10. w23.08 8 ¶3-4
Lolemba, September 1
Kuwala kwam’mawa kudzatifikira kuchokera kumwamba.—Luka 1:78.
Mulungu wapatsa Yesu mphamvu zothetsa mavuto onse a anthu. Pochita zozizwitsa, Yesu anasonyeza kuti ali ndi mphamvu zothetsera mavuto omwe sitingathe kuwathetsa patokha. Mwachitsanzo, iye ali ndi mphamvu yotipulumutsa ku zimene zinayambitsa mavuto a anthu, zomwe ndi uchimo umene tinatengera komanso zotsatirapo zake monga matenda ndi imfa. (Mat. 9:1-6; Aroma 5:12, 18, 19) Zozizwitsa zomwe anachita, zimasonyeza kuti iye angathe kuchiritsa “matenda amtundu uliwonse” ngakhalenso kuukitsa akufa. (Mat. 4:23; Yoh. 11:43, 44) Alinso ndi mphamvu yotha kuletsa mphepo zamkuntho komanso kugonjetsa mizimu yoipa. (Maliko 4:37-39; Luka 8:2) N’zolimbikitsa kudziwa kuti Yehova wapatsa Mwana wake mphamvu zochitira zimenezi. Sitikayikira kuti malonjezo omwe tikuyembekezera mu Ufumu wa Mulungu adzakwaniritsidwa. Zozizwitsa zimene Yesu anachita ali munthu padzikoli, zimatiphunzitsa kuti monga Mfumu ya Ufumu wa Mulungu, adzachita zambiri m’tsogolomu. w23.04 3 ¶5-7