Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Kulambira Makolo
    Kukambitsirana za m’Malemba
    • Kodi nkwayani kumene kulambira kwathu kuyenera kulunjikitsidwako?

      Luka 4:8, NW: “Yesu anati kwa iye: ‘Kwalembedwa, “Ndiye Ambuye Mulungu wako uyenera kumlambira, ndipo ndi kwa iye yekha uyenera kuperekako utumiki wopatulika.”’”

      Yoh. 4:23, 24: “Ikudza nthaŵi, ndipo tsopano iripo, imene olambira owona adzalambira Atate mu mzimu ndi m’chowonadi; pakuti Atate afuna otere akhale olambira ake. Mulungu ndiye mzimu; ndipo omlambira iye ayenera kumlambira mu mzimu ndi m’chowonadi.”

      Kodi nchiyembekezo chotani chimene chiripo kaamba ka mtsogolo cha kugwirizanitsa ziŵalo zabanja, kuphatikizapo awo amene anafa?

      Yoh. 5:28, 29: “Musazizwe ndi ichi, kuti ikudza nthaŵi imene onse ali m’manda adzamva mawu ake, nadzatulukira, amene adachita zabwino, kukuuka kwa moyo; koma amene anachita zoipa kukuuka kwa kuŵeruza.”

  • Kulambira Mizimu
    Kukambitsirana za m’Malemba
    • Kulambira Mizimu

      Tanthauzo: Chikhulupiriro chakuti mbali ya mzimu ya anthu imapulumuka imfa yathupi laumunthu ndipo ingakhoze kulankhulana ndi amoyo, kaŵirikaŵiri kupyolera mwa munthu amene amatumikira monga wobwebweta. Anthu ena amakhulupirira kuti zinthu zonse zakuthupi ndi zochitika zonse za chilengedwe ziri ndi mizimu yokhalamo. Kupenduza ndiko kugwiritsiridwa ntchito kwa mphamvu imene imavomerezedwa kukhala yochokera kwa mizimu yoipa. Mipangidwe yonse ya kukhulupirira mizimu imatsutsidwa mwamphamvu m’Baibulo.

      Kodi kulidi kotheka kwa munthu kulankhulana ndi “mzimu” wa wokondedwa wakufa?

      Mlal. 9:5, 6, 10: “Amoyo adziŵa kuti tidzafa; koma akufa sadziŵa kanthu bi . . . Chikondi chawo ndi mdano wawo ndi dumbo lawo lomwe zatha tsopano; ndipo nthaŵi yamuyaya sagaŵa konse kanthu kalikonse kachitidwa pansi pano. Chirichonse dzanja lako lichipeza kuchichita, uchichite ndi mphamvu yako; pakuti mulibe ntchito ngakhale kulingirira ngakhale kudziŵa, ngakhale nzeru, [ku Sheoli] kumanda uli kupitako.”

      Ezek. 18:4, 20: “Moyo wochimwawo ndiwo udzafa.” (Motero moyo sindiwo kanthu kena kamene kamapulumuka imfa yathupi ndi kamene pambuyo pake anthu amoyo angalankhulane nako.)

      Sal. 146:4: “Mpweya [mzimu (NW)] wake uchoka, abwerera kumka kunthaka yake; tsiku lomwelo zotsimikiza mtima zake zitayika.” (Pamene mzimu unenedwa kuti ‘uchoka’ m’thupi, imeneyi iri kokha njira ina ya kunena kuti mphamvu ya moyo yaleka kugwira ntchito. Motero, munthu atafa, mzimu wake sumakhalako monga chinthu chapadera chimene chingalingalire ndi kukwaniritsa zolinganiza popanda thupi. Uwo sindiwo kanthu kena kamene amoyo angalankhulane nako pambuyo pa imfa ya munthuyo.)

      Wonaninso tsamba 153-155, pamutu wakuti “Imfa.”

      Kodi Baibulo silimasonyeza kuti Mfumu Sauli analankhulana ndi mneneri Samueli pambuyo pa imfa ya Samueli?

      Cholembedwacho chikupezeka pa 1 Samueli 28:3-20. Vesi 13, 14 imasonyeza kuti Sauli sanawone Samueli koma anangoyerekezera kokha mwa malongosoledwe operekedwa ndi wowombedzayo akuti iye anawona Samueli. Mothedwa nzeru Sauli anafuna kukhulupirira kuti anali Samueli ndipo motero anadzichititsa kuti anyengedwe. Vesi 3 limanena kuti Samueli anali wakufa ndi woikidwa m’manda. Malemba ogwidwa mawu m’mutu wankhani waung’ono wapitawo amamveketsa bwino kuti panalibe mbali ya Samueli imene inali moyo m’dziko lina ndi imene inali yokhoza kulankhulana ndi Sauli. Liwu limene linayeserera kukhala la Samueli linali la wonyenga.

      Kodi ndani amene awo oyesayesa kulankhula ndi akufa kwenikweni amalankhulana nawo?

      Chowonadi cha mkhalidwe wa akufa chalongosoledwa momvekera bwino m’Baibulo. Koma kodi ndani amene anayesa kunyenga anthu aŵiri oyamba ponena za imfa? Satana anatsutsa chenjezo la Mulungu lakuti kusamvera kukadzetsa imfa. (Gen. 3:4; Chiv. 12:9) Ndithudi, m’nthaŵi yokwanira, kunafikira kukhala kwachiwonekere kuti anthu anafa monga momwe Mulungu ananenera kuti akatero. Pamenepo, moyenerera, kodi ndani amene anali ndi thayo la kupeka lingaliro lakuti anthu samafadi koma kuti mbali ina ya munthu imapulumuka imfa yathupi? Chinyengo chotero chimayenera Satana Mdyerekezi, amene Yesu analongosola kukhala “atate wake wabodza.” (Yoh. 8:44; wonaninso 2 Atesalonika 2:9, 10.) Chikhulupiriro chakuti akufa alidi amoyo m’chigawo china ndi kuti tingathe kulankhulana nawo sichinapindulitse anthu. Mmalo mwake, Chivumbulutso 18:23 chimanena kuti, kupyolera mwa machitachita a kukhulupirira mizimu a Babulo Wamkulu, “mitundu yonse inasokeretsedwa.” Machitachita a kukhulupirira mizimu a ‘kulankhula ndi akufa’ alidi chinyengo cha machenjera chimene chingaike anthu m’chigwirizano ndi ziŵanda (angelo amene anakhala adyera napandukira Mulungu) ndipo kaŵirikaŵiri amatsogolera ku kumva mawu osafunika ndi kuukiridwa ndi mizimu yoipa imeneyo kwa munthuyo.

      Kodi pali chivulazo m’kufunafuna mankhwala kapena chitetezo mwanjira ya kukhulupirira mizimu?

      Agal. 5:19-21: “Ntchito zathupi ziwonekera, ndizo dama, chodetsa, kukhumba zonyansa, kupembedza mafano, nyanga . . . zimene ndikuchenjezani nazo, monga ndachita, kuti iwo akuchitachita zotere sadzaloŵa Ufumu wa Mulungu.” (Kutembenukira ku kukhulupirira mizimu kaamba ka chithandizo kumatanthauza kuti munthuyo akukhulupirira mabodza a Satana ponena za imfa; iye akufunafuna uphungu kwa anthu amene amayesayesa kupeza mphamvu kuchokera kwa Satana ndi ziŵanda zake. Motero munthu woteroyo amadzigwirizanitsa ndi awo amene ali adani odziŵika a Yehova Mulungu. Mmalo mwa kuthandizidwadi, yense wa kupitirizabe m’njira yotero amakhala ndi chivulazo chosatha.)

      Luka 9:24: “Amene aliyense akafuna kupulumutsa moyo wake [kapena, umoyo], iye adzautaya; koma amene aliyense akataya moyo wake chifukwa cha ine [chifukwa chakuti ali wotsatira wa Yesu Kristu], iye adzaupulumutsa uwu.” (Ngati mwadala munthu aswa malamulo olongosoledwa momvekera bwino a Mawu a Mulungu m’kuyesayesa kutetezera kapena kusunga moyo wake wamakono, adzatayikiridwa ndi chiyembekezo cha moyo wamuyaya. Ha nkupusa kotani nanga!)

      2 Akor. 11:14, 15: “Satana yemwe adziwonetsa ngati mngelo

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena