Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Baibulo
    Kukambitsirana za m’Malemba
    • m’Baibulo. (2 Tim. 3:16, 17)’ (2) ‘Mulungu samafuna kuti tipwayirepwayire mosadziŵa; iye wanena kuti chifuniro chake kwa ife nchakuti tifike pa chidziŵitso cholongosoka cha chowonadi. (1 Tim. 2:3, 4) Mwanjira yokhutiritsa kwambiri Baibulo limayankha funso longa lakuti . . . ’ (Kuthandiza anthu ena, inu choyamba mungafunikire kukambitsirana umboni wa kukhulupirira kukhalapo kwa Mulungu. Wonani tsamba 306-313, pamutu wakuti “Mulungu.”)

      ‘Baibulo ndibukhu la azungu’

      Mungayankhe kuti: ‘Nzowonadi kuti iwo asindikiza makope ambiri a Baibulo. Koma Baibulo silimanena kuti fuko lina ndilabwino kwambiri koposa lina.’ Ndiyeno mwinamwake wonjezerani kuti: (1) ‘Baibulo nlochokera kwa Mlengi wathu, ndipo iye ngwopanda tsankho. (Mac. 10:34, 35)’ (2) ‘Mawu a Mulungu amalonjeza mwaŵi wa kukhala ndi moyo kosatha pansi pano pansi pa Ufumu wake kwa anthu amitundu yonse ndi mafuko. (Chiv. 7:9, 10, 17)’

      Kapena munganene kuti: ‘Kutalitali! Mlengi wa anthu ndiye amene anasankha amuna amene akawauzira kulemba mabukhu 66 a Baibulo. Ndipo ngati anasankha kugwiritsira ntchito anthu akhungu loyera, limenelo linali thayo lake. Koma uthenga wa Baibulo sunali wa anthu oyera okha.’ Ndiyeno mwinamwake wonjezerani kuti: (1) ‘Wonani chimene Yesu ananena . . . (Yoh. 3:16) “Yense” amaphatikizapo anthu a khungu lamawonekedwe ali onse. Ndiponso, asanakwere kumwamba, Yesu ananena mawu otsazikira awa kwa ophunzira ake . . . (Mat. 28:19)’ (2) ‘Mokondweretsa, Machitidwe 13:1 amanena za munthu wina wotchedwa Nigeri, dzina limene limatanthauza kuti “wakuda.” Iye anali mmodzi wa aneneri ndi aphunzitsi ampingo wa Antiokeya, Siriya.’

      ‘Ndimakhulupirira kokha King James Version’

      Mungayankhe kuti: ‘Ngati lanu liri pafupi, ndingakonde kugaŵana nanu kanthu kena kamene ndakawona kukhala kolimbikitsa kwambiri.’

      Kapena munganene kuti: ‘Anthu ambiri amagwiritsira ntchito matembenuzidwe amenewo a Baibulo, ndipo ine mwinine ndiri nalo m’laibulale langa.’ Ndiyeno mwinamwake wonjezerani kuti: (1) ‘Kodi munadziŵa kuti pachiyambiyambi Baibulo linalembedwa m’chinenero Chachihebri, Chachiaramu, ndi Chigiriki? . . . Kodi inu mumaŵerenga zinenero zimenezo? . . . Chotero tiri okondwera kuti Baibulo latembenuzidwira m’Chicheŵa.’ (2) ‘Tchati ichi (“Mpambo wa Mabukhu a Baibulo,” mu NW) chimasonyeza kuti Genesis, bukhu loyamba la Baibulo, linamalizidwa mu 1513 B.C.E. Kodi munadziŵa, kuti pambuyo pa kulembedwa kwa Genesis, panapita zaka 2 900 Baibulo lonse lathunthu lisanatembenuziridwe m’Chingelezi? Ndipo zoposa zaka 200 zinapita matembenuzidwe a King James Version asanamalizidwe (1611 C.E.).’ (3) ‘Kuyambira zaka za zana la 17, Chingelezi chakhala ndi masinthidwe ambiri. Tawona zimenezo m’nthaŵi ya moyo wathu, kodi sichoncho? . . . Chotero tikuyamikira matembenuzidwe amakono amene amasonyeza mosamalitsa chowonadi choyambirira chimodzimodzicho m’chinenero chimene timalankhula makono.’

      ‘Muli ndi Baibulo lanu’

      Wonani mutu waukulu wakuti “New World Translation.”

  • Boma
    Kukambitsirana za m’Malemba
    • Boma

      Tanthauzo: Kakonzedwe ka anthu kopangira ndi kugwiritsira ntchito malamulo. Kaŵirikaŵiri maboma amadziŵikitsidwa mogwirizana ndi magwero ndi ukulu wa ulamuliro wawo. Yehova Mulungu ndiye Wolamulira Wachilengedwe chonse, amene amapereka ulamuliro pa ena mogwirizana ndi chifuniro chake ndi chifuno. Komabe, Satana Mdyerekezi, wopandukira ulamuliro wa Yehova wamkulu, ali ‘wolamulira wa dziko’—mololedwa ndi Mulungu kwa kanthaŵi. Baibulo limasonyeza dongosolo ladziko lonse la ulamuliro wandale zadziko kukhala chirombo ndipo limanena kuti “chinjoka [Satana Mdyerekezi] chinampatsa [chirombo] mphamvu yake, ndi mpando wake wachifumu, ndi ulamuliro waukulu.”—Yoh. 14:30; Chiv. 13:2; 1 Yoh. 5:19.

      Kodi nkotheka kwa anthu kukhazikitsa boma limene lidzabweretsadi chimwemwe chosatha?

      Kodi cholembedwa cha mbiri ya anthu chimasonyezanji?

      Mlal. 8:9: “Wina apweteka mzake pomlamulira.” (Zimenezi ziridi zowona ngakhale kuli kwakuti maboma ena ndi olamulira anayamba ndi chitsanzo chabwino.)

      “Chitaganya chirichonse chimene chinaliko potsirizira pake

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena