Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • lfb phunziro 6 tsamba 20-tsamba 21 ndime 5
  • Anthu 8 Anapulumuka

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Anthu 8 Anapulumuka
  • Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
  • Nkhani Yofanana
  • Madzi Alisesa Dziko
    Kumamumvetsera Mphunzitsi Wamkuru’yo
  • Chingalawa cha Nowa
    Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
  • Chigumula Chachikulu
    Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
  • Nowa Akhoma Chingalawa
    Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
Onani Zambiri
Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
lfb phunziro 6 tsamba 20-tsamba 21 ndime 5
Mvula ikugwa ndipo chingalawa chikuyandama

MUTU 6

Anthu 8 Anapulumuka

Nowa ndi banja lake akutuluka m’chingalawa

Nowa ndi banja lake analowa m’chingalawa limodzi ndi nyama. Yehova anatseka chitseko cha chingalawacho ndipo mvula inayamba kugwa. Mvulayo inali yambiri moti chingalawa chija chinayamba kuyandama. Kenako madzi anamiza nthaka yonse. Anthu oipa onse amene anali kunja kwa chingalawacho anafa. Koma Nowa ndi banja lake anapulumuka. Iwo ayenera kuti anasangalala kwambiri podziwa kuti anamvera Yehova.

Mvulayo inagwa kwa masiku 40, masana ndi usiku. Kenako inasiya ndipo madzi anayamba kuphwera. Ndiyeno chingalawacho chinaima paphiri. Koma padzikoli panali padakali madzi ambiri, choncho Nowa ndi banja lakelo anakhalabe m’chingalawacho.

Madziwo ankaphwera pang’onopang’ono. Nowa ndi banja lakelo anakhala m’chingalawacho kupitirira chaka chimodzi. Kenako Yehova anawauza kuti atuluke ndipo zinali ngati akulowa m’dziko latsopano. Iwo anathokoza kwambiri Yehova chifukwa chowapulumutsa moti anapereka nsembe.

Utawaleza

Yehova anasangalala kwambiri ndi nsembeyo. Iye analonjeza kuti sadzagwiritsanso ntchito chigumula powononga zinthu padzikoli. Potsimikizira zimenezi, anachititsa kuti kumwamba kuoneke utawaleza woyambirira. Kodi iweyo unaonapo utawaleza?

Kenako Yehova anauza Nowa ndi banja lake kuti akhale ndi ana n’kudzaza dziko lapansi.

“Nowa analowa mʼchingalawa. Anthu ananyalanyaza zimene zinkachitika mpaka Chigumula chinafika nʼkuwaseseratu onsewo.”​—Mateyu 24:38, 39

Mafunso: Kodi chinachitika n’chiyani Yehova atatseka chitseko cha chingalawa? Kodi tiyenera kukumbukira chiyani tikaona utawaleza?

Genesis 7:1-24; 8:1-22; 9:1-17

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena