Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • lfb phunziro 7 tsamba 24-tsamba 25 ndime 1
  • Nsanja ya ku Babele

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Nsanja ya ku Babele
  • Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
  • Nkhani Yofanana
  • Anthu Amanga Chinsanja
    Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
  • Kodi Zinenero Zathu Zinayambira pa “Nsanja ya Babele”?
    Nsanja ya Olonda—2013
  • Nsanja ya Babele Yamakono?
    Galamukani!—1987
  • Chingalawa cha Nowa
    Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
Onani Zambiri
Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
lfb phunziro 7 tsamba 24-tsamba 25 ndime 1
Yehova wasokoneza chinenero ndipo anthu sakuthanso kumangira limodzi Nsanja ya ku Babele

MUTU 7

Nsanja ya ku Babele

Chigumula chitatha, ana a Nowa anabereka ana ambiri. Choncho anawo anayamba kukhala m’madera osiyanasiyana padziko lapansi. Izi ndi zimene Yehova anawauza.

Koma panali anthu ena amene sanamvere Yehova. Iwo anauzana kuti: ‘Tiyeni timange mzinda kuti tizingokhala pompano. Timange nsanja yaitali yoti mpaka ikafike kumwamba. Tikatero titchuka.’

Yehova sanasangalale ndi zimene anthuwa ankachita ndipo anaganiza zowaletsa. Kodi ukudziwa zimene anachita? Yehova anachititsa kuti mwadzidzidzi anthuwo ayambe kulankhula zilankhulo zosiyanasiyana. Popeza sankathanso kumvana, anasiya ntchito yomangayo. Mzinda umene ankamangawo unatchedwa Babele kutanthauza “Chisokonezo.” Ndiyeno anthuwo anayamba kuchoka n’kumakakhala m’malo osiyanasiyana padziko lapansili. Koma anapitirizabe kuchita zoipa m’madera osiyanasiyana amene ankakhala. Kodi panali ena amene ankakondabe Yehova? Tikambirana zimenezi m’mutu wotsatira.

“Aliyense wodzikweza adzachititsidwa manyazi, koma aliyense amene amadzichepetsa adzakwezedwa.”​—Luka 18:14

Mafunso: Kodi anthu a ku Babele anachita chiyani? Kodi Yehova anawaletsa bwanji?

Genesis 11:1-9

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena