Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • g 3/14 tsamba 8-9
  • Ndalama

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Ndalama
  • Galamukani!—2014
  • Timitu
  • Nkhani Yofanana
  • Kodi ndalama ndi zimene zimabweretsa mavuto onse?
  • Kodi ndalama zimathandiza bwanji?
  • Kodi mungatani kuti muzigwiritsa ntchito bwino ndalama?
  • Kodi Ndalama ndi Zimene Zimabweretsa Mavuto Onse?
    Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
  • Kodi Mungatani Kuti Musakhale Wokonda Ndalama?
    Galamukani!—2015
  • Tiziona Ndalama Moyenera
    Galamukani!—2007
  • Muzigwiritsa Ntchito Bwino Ndalama
    Banja Lanu Likhoza Kukhala Losangalala
Onani Zambiri
Galamukani!—2014
g 3/14 tsamba 8-9
Mulu wa ndalama

ZIMENE BAIBULO LIMANENA

Ndalama

Kodi ndalama ndi zimene zimabweretsa mavuto onse?

“Kukonda ndalama ndi muzu wa zopweteka za mtundu uliwonse.”—1 Timoteyo 6:10.

ZIMENE ENA AMANENA

Ndalama ndi zimene zimabweretsa mavuto onse.

ZIMENE BAIBULO LIMANENA

“Kukonda ndalama,” osati ndalama zenizenizo, n’kumene kumayambitsa mavuto a “mtundu uliwonse.” Baibulo limanena kuti Mfumu Solomo, amene anali wolemera, anatchula mavuto atatu amene anthu okonda ndalama amakumana nawo. Vuto loyamba: Amakhala ndi nkhawa. Lemba la Mlaliki 5:12 limati: “Zambiri zimene munthu wolemera amakhala nazo zimamulepheretsa kugona.” Vuto lachiwiri: Kusakhutitsidwa. Lemba la Mlaliki 5:10 limanena kuti: “Munthu wokonda siliva sakhutira ndi siliva, ndipo wokonda chuma sakhutira ndi phindu limene amapeza.” Vuto lachitatu: Zimakhala zosavuta kuti aphwanye malamulo. Lemba la Miyambo 28:20 limati: “Woyesetsa kuti apeze chuma mofulumira, sadzapitiriza kukhala wosalakwa.”

Kodi ndalama zimathandiza bwanji?

‘Ndalama zimateteza.’—Mlaliki 7:12.

ZIMENE ENA AMANENA

Ndalama zimateteza komanso zimapangitsa munthu kukhala wosangalala.

ZIMENE BAIBULO LIMANENA

Mfundo yoti ndalama zimapangitsa munthu kukhala wosangalala komanso wotetezeka ndi bodza lamkunkhuniza. (Maliko 4:19) Komabe ngakhale zili choncho, Baibulo limati “ndalama zimathandiza pa zinthu zonse” zofunika pa moyo. (Mlaliki 10:19) Mwachitsanzo, tingagwiritse ntchito ndalama kugula zinthu zimene zingatithandize kuti tikhale ndi moyo monga chakudya komanso mankhwala.—2 Atesalonika 3:12.

Mungagwiritsenso ntchito ndalama kusamalira banja lanu. Ndipotu Baibulo limati: “Ngati munthu sasamalira anthu amene ndi udindo wake kuwasamalira, makamaka a m’banja lake, wakana chikhulupiriro ndipo ndi woipa kuposa munthu wosakhulupirira.”—1 Timoteyo 5:8.

Kodi mungatani kuti muzigwiritsa ntchito bwino ndalama?

‘Muzikhala pansi n’kuwerengera ndalama zimene mungawononge.’—Luka 14:28.

ZIMENE BAIBULO LIMANENA

Muzigwiritsa ntchito ndalama m’njira imene Mulungu amavomereza. (Luka 16:9) Ndi bwino kugwiritsa ntchito ndalama mwanzeru komanso mopanda chinyengo. (Aheberi 13:18) Kutsatira malangizo oti “moyo wanu ukhale wosakonda ndalama,” kungakuthandizeni kuti musamawononge ndalama zoposa zimene mumapeza.—Aheberi 13:5.

Ngakhale kuti Baibulo sililetsa ngongole, limatichenjeza kuti: “Wobwereka amakhala kapolo wa wobwereketsayo.” (Miyambo 22:7) Muzipewa kugula zinthu musanakonzekere, chifukwa “aliyense wopupuluma, ndithu adzasauka.” (Miyambo 21:5) M’malomwake, ‘muziika kenakake pambali kunyumba kwanu malinga ndi mmene zinthu zikuyendera pa moyo wanu.’—1 Akorinto 16:2.

Baibulo limatilimbikitsa kuti ‘tikhale opatsa.’ (Luka 6:38) Anthu amene amafuna kukondweretsa Mulungu amaona kuti ndi bwinodi kukhala owolowa manja chifukwa “Mulungu amakonda munthu wopereka mokondwera.” (2 Akorinto 9:7) Choncho, “musaiwale kuchita zabwino ndi kugawana zinthu ndi ena, pakuti nsembe zotero Mulungu amakondwera nazo.”—Aheberi 13:16.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena