Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w04 10/15 tsamba 3
  • Kusakasaka Chuma

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kusakasaka Chuma
  • Nsanja ya Olonda—2004
  • Nkhani Yofanana
  • Pindulani Polimbikira Kuchita Zinthu Zauzimu
    Nsanja ya Olonda—2004
  • Maphunziro a Pakoleji—Kukonzekera Kaamba ka Chiyani?
    Galamukani!—1987
  • Kufunafuna Dongosolo Ladziko Latsopano
    Nsanja ya Olonda—1991
  • Kuteteza Dzina Lathu Monga Akristu
    Nsanja ya Olonda—2005
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda—2004
w04 10/15 tsamba 3

Kusakasaka Chuma

“Ngati tili ndi mtima womangofuna chuma, sitingakhutitsidwe nacho,” linatero lipoti la Worldwatch Institute.

“KODI tikufuna chiyani? Zinthu zonse. Kodi tikuzifuna liti? Pomwe pano.” Mawu ameneŵa anali otchuka kwa ophunzira ena akukoleji m’zaka za m’ma 1960. Masiku ano, mwina sikumveka mawu ofanana ndendende ndi mawuŵa, koma mfundo ya mawu ameneŵa imamvekabe. Inde, zikuoneka kuti anthu ambiri masiku athu ano ali ndi mtima wosakasaka chuma chambiri.

Kwa anthu ambiri, kupeza chuma ndiponso zinthu zambiri ndi chimodzi mwa zinthu zofunika kwambiri pamoyo wawo. Pulezidenti wakale wa dziko la America, Jimmy Carter, nthaŵi ina anati: “Anthu masiku ano sadziŵikanso ndi zimene amachita koma ndi zimene ali nazo.” Kodi zilipo zinthu zofunika kwambiri kuposa chuma? Ngati zilipo, kodi zinthu zake n’chiyani, nanga n’zopindulitsa bwanji?

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena