-
Yehova Amawerenga ‘Tsitsi Lonse la M’mutu Mwanu’Nsanja ya Olonda—2005 | August 1
-
-
6 Pofuna kuthandiza atumwi ake kumvetsetsa chifukwa chimene sayenera kuchitira mantha, Yesu anapereka mafanizo awiri. Iye anawauza kuti: ‘Kodi mpheta ziwiri sizigulidwa kakobiri? Ndipo imodzi ya izo siigwa pansi popanda Atate wanu [kudziwa]: komatu inu, tsitsi lonse la m’mutu mwanu amaliwerenga. Chifukwa chake musamawopa; inu mupambana mpheta zambiri.’ (Mateyu 10:29-31) Onani kuti malingana ndi mawu a Yesuwa, kuti tisachite mantha pa mavuto m’pofunika kuti tisamakayikire kuti Yehova amatiganizira ifeyo patokha. Zikuoneka kuti mtumwi Paulo sankakayikira mfundo imeneyi. Iye analemba kuti: “Ngati Mulungu ali ndi ife, adzatikaniza ndani? Iye amene sanatimana Mwana wake wa iye yekha, koma anam’pereka chifukwa cha ife tonse, adzalekeranji kutipatsanso ife zinthu zonse kwaulere pamodzi ndi iye?” (Aroma 8:31, 32) Ngakhale mutakumana ndi mavuto aakulu motani, inunso panokha musamakayikire ngakhale pang’ono kuti Yehova amakuganizirani panthawi yonse imene muli wokhulupirika kwa iye. Poona mwatsatanetsatane mawu amene Yesu ananena polimbikitsa atumwi ake, titsimikizira mfundo imeneyi.
Mtengo wa Mpheta
7, 8. (a) Kodi anthu ankaziona bwanji mpheta m’nthawi ya Yesu? (b) Kodi zikuoneka kuti n’chifukwa chiyani pa Mateyu 10:29 pali mawu a Chigiriki otanthauza kuti “timpheta”?
7 Mafanizo a Yesu amasonyeza bwino mfundo yakuti Yehova amaganizira atumiki Ake onse paokhapaokha. Poyamba taganizirani fanizo la mpheta lija. M’masiku a Yesu, mpheta zinali ndiwo, koma chifukwa choti zinkawononga mbewu, kwenikweni anthu ankaziona ngati mbalame zowononga. Mpheta zinalipo zambiri ndiponso zotsika mtengo kwambiri moti ziwiri zinkagulitsidwa pa mtengo wangati umene timagulira machesi masiku ano. Ndalama zochuluka mowirikiza kawiri kuposa pamenepo ankagulira mpheta zisanu osati zinayi zokha ayi. Mpheta inayo inkangokhala ya basela basi, ngati kuti inali yosawerengeredwa n’komwe.—Luka 12:6.
8 Taganiziraninso za kukula kwa mphetazi, zomwe zinali mbalame wamba. Poyerekezera ndi mbalame zina zambiri, ngakhale mpheta yoti yakula kufika pamapeto imakhala yaing’ono kwambiri. Komatu mawu a Chigiriki omwe anawamasulira kuti “mpheta” pa Mateyu 10:29 amanena makamaka za timpheta tating’onoting’ono. Apa zikuoneka kuti Yesu ankafuna kuti atumwi ake aganizire za mbalame yaing’ono kwambiri ndiponso yotsika mtengo kwambiri.
9. Kodi chitsanzo chimene Yesu anapereka cha mpheta chili ndi mfundo yotani yogwira mtima kwambiri?
9 Chitsanzo cha mpheta chimene Yesu ananenachi chimatithandiza kumvetsa mfundo yofunika kwambiri yakuti: Zinthu zimene zimaoneka ngati zosafunika kwa anthu n’zofunika kwa Yehova Mulungu. Yesu anapitiriza kugogomezera mfundo imeneyi powonjezera kunena kuti ngakhale mpheta yaing’ono “siigwa pansi” popanda Yehova kuona.c Pamenepatu pali phunziro lomveka bwino. Ngati Yehova Mulungu amaona kambalame kakang’ono ndiponso kosawerengeredwa n’komwe kameneka, kodi angalephere bwanji kuganizira mavuto a munthu amene akum’tumikira?
-
-
Yehova Amawerenga ‘Tsitsi Lonse la M’mutu Mwanu’Nsanja ya Olonda—2005 | August 1
-
-
c Anthu ena ophunzira mozama amati kugwa pansi kwa mphetaku n’kutheka kuti sikukutanthauza chabe kufa kwa mphetazo. Amati mawu a Chigirikiwo angathe kutanthauza za kufika pansi kwa mbalameyo ikamatera kuti idye chakudya. Ngati tanthauzo la mawu amenewa lili limeneli, ndiye kuti Mulungu amaona ndiponso amasamalira mbalamezi pa zochitika zawo zonse za tsiku n’tsiku, osati zikangofa chabe ayi.—Mateyu 6:26.
-