Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2017
mwb17 December tsamba 5
MOYO WATHU WACHIKHRISTU
Mbali Yatsopano pa Misonkhano ya Mkati mwa Mlungu
Kuyambira m’mwezi wa January 2018, pa misonkhano ya mkati mwa mlungu padzakhala gawo lokhala ndi mfundo, zithunzi, mavidiyo ndi zinthu zina. Zinthu zimenezi zikupezeka mu Baibulo la Dziko Latsopano lachingelezi la Study Edition la pa intaneti. Tidzakhala ndi gawoli ngakhale kuti tilibe Baibulo la Study Edition m’chinenero chathu. Sitikukayikira kuti zinthu zimenezi zidzakuthandizani kwambiri pokonzekera misonkhano. Komanso chofunika kwambiri n’chakuti zidzakuthandizani kuti muyandikire Atate wathu wachikondi Yehova.