-
‘Khalanibe M’mawu Anga’Nsanja ya Olonda—2003 | February 1
-
-
16. (a) Kodi ndi anthu otani amene amafanana ndi nthaka yaminga? (b) Malinga ndi nkhani za m’Mauthenga Abwino atatu, kodi minga imaimira chiyani?—Onani mawu a munsi.
16 Kodi ndi anthu otani amene amafanana ndi nthaka yaminga? Yesu akufotokoza kuti: “Ndiwo amene adamva, ndipo m’kupita kwawo atsamwitsidwa ndi nkhaŵa, ndi chuma, ndi zokondweretsa za moyo, ndipo sakhwimitsa zipatso zamphumphu.” (Luka 8:14) Monga mmene mbewu za wofesa ndiponso minga zimakulira m’nthaka panthaŵi imodzi, chotero anthu ena amayesa kutenga mawu a Mulungu ndiponso ‘zokondweretsa za moyo uno’ panthaŵi imodzi. Choonadi cha mawu a Mulungu chimafesedwa m’mitima yawo, koma chimalimbana ndi zinthu zina zimene zimafuna kuti iwo azisamalire. Mtima wawo wophiphiritsa umagaŵikana. (Luka 9:57-62) Zimenezi zimawalepheretsa kukhala ndi nthaŵi yokwanira yosinkhasinkha mawu a Mulungu mwapemphero ndiponso mopindulitsa. Iwo amalephera kuphunzira mokhazikika mawu a Mulungu ndipo motero sayamikira kuchokera pansi pamtima, chinthu chomwe n’chofunika kuti apirire. Pang’onopang’ono, zinthu zauzimu zimene amakonda zimaphimbidwa ndi zinthu zosakhala zauzimu moti zimafika ‘potsamwitsidwa’ kotheratu.c Ameneŵa amakhala mapeto omvetsa chisoni a anthu amene sakonda Yehova ndi mtima wonse.—Mateyu 6:24; 22:37.
17. Kodi tiyenera kuchita chiyani m’moyo kuti tisatsamwitsidwe ndi minga yophiphiritsa imene yatchulidwa m’fanizo la Yesu?
17 Mwa kukonda kwambiri zinthu zauzimu kuposa zakuthupi, timapeŵa kutsamwitsidwa ndi mavuto ndi zokondweretsa za dziko lino. (Mateyu 6:31-33; Luka 21:34-36) Sitiyenera kunyalanyaza kuŵerenga Baibulo ndi kusinkhasinkha zimene taŵerengazo. Tidzapeza nthaŵi yochuluka ya kusinkhasinkha moyikirapo mtima ndi mwapemphero ngati tifeŵetsa moyo wathu mmene tingathere. (1 Timoteo 6:6-8) Yehova akudalitsa atumiki ake amene tinganene kuti, achotsa minga panthaka kuti apatse chakudya chambiri, kuŵala ndi malo ku mbewu yobala zipatso. Sandra wa zaka 26 anati: “Ndikasinkhasinkha madalitso anga m’choonadi, ndimazindikira kuti palibe chimene dziko lingapereke chimene chingafanane ndi choonadi.”—Salmo 84:11.
-
-
‘Khalanibe M’mawu Anga’Nsanja ya Olonda—2003 | February 1
-
-
c Malinga ndi nkhani za m’Mauthenga Abwino atatu za fanizo la Yesu, mbewu zinatsamwitsidwa ndi mavuto ndi zokondweretsa za dziko lino. Nkhanizo zimati zimenezi zinali: “Malabadiro a dziko lapansi,” “chinyengo cha chuma,” “kulakalaka kwa zinthu zina,” ndi “zokondweretsa za moyo.”—Marko 4:19; Mateyu 13:22; Luka 8:14; Yeremiya 4:3, 4.
-