-
“Dziwani Kuti Ine Ndili Pamodzi ndi Inu Masiku Onse”Nsanja ya Olonda—2013 | July 15
-
-
13. Kodi lemba la Chivumbulutso 18:7 likusonyeza kuti panopa hule, kapena kuti Babulo Wamkulu, kuphatikizapo matchalitchi amene amati ndi achikhristu, akutani?
13 Chachitatu ndi kulira ndi kukukuta mano. Kodi anthu okhala ngati namsongole akadzamangidwa m’mitolo chidzawachitikire n’chiyani? Yesu ananena kuti: “Kumeneko adzalira ndi kukukuta mano.” (Mat. 13:42) Kodi zimenezi zikuchitika panopa? Ayi. Matchalitchi amene amati ndi achikhristu, omwe ndi mbali ya hule, akunenabe kuti: “Ine ndine mfumukazi. Sindine mkazi wamasiye, ndipo sindidzalira ngakhale pang’ono.” (Chiv. 18:7) N’zoona kuti matchalitchi amenewa akudziona kuti ndi amphamvu ndipo ali ngati mfumukazi yolamulira atsogoleri andale. Masiku ano, anthu amene ali ngati namsongole sakulira koma akudzitama. Komabe zinthu zisintha posachedwapa.
Posachedwapa matchalitchi amene amati ndi achikhristu ndiponso atsogoleri andale adzasiya kugwirizana (Onani ndime 13)
14. (a) Kodi mawu akuti Akhristu onyenga ‘adzakukuta mano awo’ akutanthauza chiyani, ndipo zidzachitika liti? (b) Kodi zimene tafotokoza zokhudza lemba la Mateyu 13:42 zikugwirizana bwanji ndi mfundo ya pa Salimo 112:10? (Onani mawu akumapeto.)
14 Pa chisautso chachikulu, zipembedzo zonse zonyenga zikadzawonongedwa, anthu onse amene ankagwirizana nazo adzayesa kubisala koma sadzapeza malo. (Luka 23:30; Chiv. 6:15-17) Iwo adzazindikira kuti awonongedwa basi chifukwa sangathe kuthawa. Pa nthawi imeneyi, adzalira chifukwa chosowa mtengo wogwira ndipo ‘adzakukuta mano’ chifukwa chokwiya. Mu ulosi wake wonena za chisautso chachikulu, Yesu ananena kuti zinthu zikadzawathina chonchi, “adzadziguguda pachifuwa chifukwa cha chisoni.”e—Mat. 24:30; Chiv. 1:7.
15. Kodi n’chiyani chidzachitikire namsongole, ndipo zidzachitika liti?
15 Chachinayi ndi kuponyedwa m’ng’anjo yamoto. Kodi n’chiyani chidzachitikire anthu omwe ali ngati mitolo ya namsongole? Angelo “adzawaponya m’ng’anjo yamoto.” (Mat. 13:42) Zimenezi zikutanthauza kuti adzawonongedweratu. Choncho, anthu onse amene ankagwirizana ndi zipembedzo zonyenga adzawonongedwa pa Aramagedo, yomwe ndi mbali yomaliza ya chisautso chachikulu.—Mal. 4:1.
-
-
“Dziwani Kuti Ine Ndili Pamodzi ndi Inu Masiku Onse”Nsanja ya Olonda—2013 | July 15
-
-
e Ndime 14: Izi zikusintha zimene tinkakhulupirira pa lemba la Mateyu 13:42. Poyamba, tinkafotokoza m’mabuku athu kuti Akhristu onyenga akhala ‘akulira ndi kukukuta mano’ kwa zaka zambiri chifukwa chakuti “ana a ufumu” akuwaulula kuti ndi “ana a woipayo.” (Mat. 13:38) Komabe Baibulo limasonyeza kuti nthawi imene anthu adzakukute mano m’pamene adzawonongedwa.—Sal. 112:10.
-