-
“Dziwani Kuti Ine Ndili Pamodzi ndi Inu Masiku Onse”Nsanja ya Olonda—2013 | July 15
-
-
16, 17. (a) Kodi Yesu anamaliza fanizo lake ndi mawu ati? (b) N’chifukwa chiyani tikunena kuti mawu amenewo adzakwaniritsidwa m’tsogolo?
16 Chachisanu ndi kuwala kwambiri. Yesu anamaliza ulosi wake ndi mawu akuti: “Pa nthawi imeneyo olungama adzawala kwambiri ngati dzuwa mu ufumu wa Atate wawo.” (Mat. 13:43) Kodi iwo adzawala liti ndiponso kuti? Ulosi umenewu udzakwaniritsidwa m’tsogolo muno. Apa Yesu analosera zinthu zimene zidzachitike kumwamba osati zimene zikuchitika masiku ano padziko lapansi.f Tikutero pa zifukwa ziwiri.
17 Chifukwa choyamba chikukhudza nthawi. Yesu anati: “Pa nthawi imeneyo olungama adzawala kwambiri.” Mawu a Yesu akuti “pa nthawi imeneyo,” ayenera kuti akunena za nthawi ya zinthu zimene anali atangotchula kumene. Iye anali atangonena kumene za ‘kuponya namsongole m’ng’anjo yamoto.’ Zimenezi zidzachitika kumapeto kwa chisautso chachikulu. Choncho odzozedwa “adzawala kwambiri” pa nthawi imeneyo. Chifukwa chachiwiri chikukhudza malo. Yesu ananena kuti olungama ‘adzawala kwambiri mu ufumu.’ Kodi zimenezi zikutanthauza chiyani? Akhristu onse odzozedwa amene adzakhalebe padzikoli mbali yoyamba ya chisautso chachikulu itatha adzakhala atadindidwa kale chidindo chomaliza. Kenako, malinga ndi ulosi wa Yesu wonena za chisautso chachikulu, iwo adzasonkhanitsidwa kumwamba. (Mat. 24:31) Kumwambako n’kumene adzawale “mu ufumu wa Atate wawo.” Ndiyeno nkhondo ya Aramagedo ikadzatha, iwo adzasangalala kwambiri kukhala m’gulu la mkwatibwi pa “ukwati wa Mwanawankhosa.”—Chiv. 19:6-9.
-
-
“Dziwani Kuti Ine Ndili Pamodzi ndi Inu Masiku Onse”Nsanja ya Olonda—2013 | July 15
-
-
f Ndime 16: Lemba la Danieli 12:3 limanena kuti “Anthu ozindikira [Akhristu odzozedwa] adzawala ngati kuwala kwa kuthambo.” Pamene iwo ali padziko lapansi, amawala akamagwira ntchito yolalikira. Komabe, lemba la Mateyu 13:43 limatchula nthawi imene adzawale kwambiri mu Ufumu wakumwamba. M’mbuyomu, tinkakhulupirira kuti malemba onse awiriwa akunena za ntchito yolalikira.
-