Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • jy mutu 22 tsamba 58-tsamba 59 ndime 6
  • Yesu Anaitana Ophunzira Ake 4

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Yesu Anaitana Ophunzira Ake 4
  • Yesu—Ndi Njira, Choonadi ndi Moyo
  • Nkhani Yofanana
  • Ophunzira Anayi Aitanidwa
    Munthu Wamkulu Woposa Onse Amene Anakhalako
  • Kutumikira Monga Asodzi a Anthu
    Nsanja ya Olonda—1992
  • Anathetsa Mantha Ndiponso Mtima Wokayikira
    Nsanja ya Olonda—2009
  • Anathetsa Mantha Ndiponso Mtima Wokayikira
    Tsanzirani Chikhulupiriro Chawo
Onani Zambiri
Yesu—Ndi Njira, Choonadi ndi Moyo
jy mutu 22 tsamba 58-tsamba 59 ndime 6
Yesu akulankhula ndi Petulo, Andireya, Yakobo ndi Yohane m’mbali mwa nyanja ya Galileya

MUTU 22

Ophunzira 4 Anakhala Asodzi a Anthu

MATEYU 4:13-22 MALIKO 1:16-20 LUKA 5:1-11

  • YESU ANAITANA OPHUNZIRA KUTI AZIMUTSATIRA NTHAWI ZONSE

  • ASODZI A NSOMBA ANAKHALA ASODZI A ANTHU

Yesu atathawa anthu a ku Nazareti omwe ankafuna kumupha anapita mumzinda wa Kaperenao. Mzindawu unali pafupi ndi nyanja ya Galileya yomwe inkadziwikanso kuti “nyanja ya Genesarete.” (Luka 5:1) Zimenezi zinakwaniritsa ulosi womwe unalembedwa m’buku la Yesaya wakuti anthu okhala m’mbali mwa nyanja ya Galileya adzaona kuwala kwakukulu.—Yesaya 9:1, 2.

Atafika ku Galileya, Yesu anapitiriza kulalikira kuti: “Ufumu wakumwamba wayandikira.” (Mateyu 4:17) Kenako Yesu anakumananso ndi ophunzira ake 4 aja. Ophunzira amenewa ndi amene ankayenda ndi Yesu koma atachoka ku Yudeya n’kubwerera kwawo anayambanso kugwira ntchito yawo yopha nsomba. (Yohane 1:35-42) Koma tsopano imeneyi inali nthawi yoti ayambe kuyenda ndi Yesu nthawi zonse ndi cholinga choti awaphunzitse mmene angamalalikirire kuti adzapitirize ntchitoyi iye atabwerera kumwamba.

Pamene Yesu ankayenda m’mbali mwa nyanja anaona Simoni Petulo ndi m’bale wake Andireya komanso anthu ena akutsuka maukonde awo. Yesu anapita pomwe panali anthuwo n’kukwera m’boti la Petulo kenako anamuuza kuti akankhire botilo m’madzi. Botilo litayenda pang’ono, Yesu anakhala pansi n’kuyamba kuphunzitsa khamu la anthu limene linali m’mbali mwa nyanjayo mfundo za choonadi zokhudza Ufumu.

Kenako Yesu anauza Petulo kuti: “Palasira kwakuya, ndipo muponye maukonde anu kuti muphe nsomba.” Koma Petulo ananena kuti: “Mlangizi, ife tagwira ntchito usiku wonse koma osapha kalikonse. Koma popeza mwanena ndinu, ndiponya maukondewa.”—Luka 5:4, 5.

Andireya, Yakobo ndi Yohane akulimbana ndi kuchotsa ukonde m’boti; Petulo wagwada pamene pali Yesu

Ataponya maukondewo, anapha nsomba zambiri moti maukonde aja anayamba kung’ambika. Nthawi yomweyo anaitana anzawo amene anali m’boti lina lapafupi kuti adzawathandize. M’kanthawi kochepa, maboti awiriwo anadzaza ndi nsomba ndipo anayamba kumira. Ataona zimenezi, Petulo anagwadira Yesu n’kunena kuti: “Ambuye, chokani pali ine pano, chifukwa ndine munthu wochimwa.” Koma Yesu anamuyankha kuti: “Usachite mantha. Kuyambira lero uzisodza anthu amoyo.”—Luka 5:8, 10.

Kenako Yesu anaitana Petulo ndi Andireya n’kuwauza kuti: “Nditsatireni, ndipo ndikusandutsani asodzi a anthu.” (Mateyu 4:19) Anaitananso asodzi ena awiri, omwe anali ana a Zebedayo ndipo mayina awo anali Yakobo ndi Yohane. Nawonso anayamba kutsatira Yesu nthawi yomweyo. Choncho anthu 4 amenewa anasiya ntchito yawo yopha nsomba ndipo anakhala ophunzira oyambirira a Yesu.

  • Kodi anthu amene Yesu anawaitana kuti akhale ophunzira ake ankagwira ntchito yotani, nanga mayina awo anali ndani?

  • Kodi Petulo anachita mantha ndi chozizwitsa chiti?

  • Kodi ophunzira 4 a Yesu anayamba usodzi wotani?

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena