Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • “Nthawi Zonse Iye Ankalankhula Nawo Pogwiritsa Ntchito Mafanizo”
    ‘Bwera Ukhale Wotsatira Wanga’
    • 13 Yesu ananenanso zinthu zina zodziwika bwino zokhudza msewu ‘wochokera ku Yerusalemu kupita ku Yeriko.’ Fanizoli limafotokoza kuti, choyamba mumsewumo munadutsa wansembe kenako Mlevi koma palibe amene anaima kuti athandize munthu wovulalayo. (Luka 10:31, 32) Ansembe ankatumikira pakachisi ku Yerusalemu ndipo Alevi ankawathandiza. Akakhala kuti sakugwira ntchito pakachisi, ansembe ndi Alevi ambiri ankakhala ku Yeriko, mzinda womwe unali pamtunda wa makilomita 23 okha kuchokera ku Yerusalemu. N’chifukwa chake ankadutsadutsa mumsewu umenewu.b N’zoonekeratu kuti pophunzitsa, Yesu ankaganizira omvera ake.

  • “Nthawi Zonse Iye Ankalankhula Nawo Pogwiritsa Ntchito Mafanizo”
    ‘Bwera Ukhale Wotsatira Wanga’
    • b Yesu ananenanso kuti wansembe ndi Mleviyo ‘ankachokera ku Yerusalemu,’ zimene zikusonyeza kuti ankachokera kukachisi. Choncho palibe amene angawaikire kumbuyo ponena kuti iwo anapewa kukhudza wovulalayo chifukwa ankaoneka ngati wafa, ndipo akanakhala osayenerera kutumikira pakachisi kwa kanthawi.​—Levitiko 21:1; Numeri 19:16.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena