-
Onjezerani Mtendere Wanu mwa Chidziwitso CholongosokaNsanja ya Olonda—1987
-
-
6. Kodi ndimotani mmene Yesu Kristu anasonyezera kuti ntchito yolalikira inali yoyambirira kwa iye?
6 Kukhala ndi chidziwitso cholongosoka cha Yesu kumafunikira kukhala ndi “maganizo a Yesu” ndi kumutsanzira iye. (1 Akorinto 2: 16) Yesu anali wolalikira wa chowonadi wanthumanzi. (Yohane 18:37) Mzimu wake wa kulalikira wamphamvu sunamangidwe ndi kunyada kwa anthu a m’mudziwo. Ngakhale kuti Ayuda ena anada a Samariya, iye anachitira umboni kwa mkazi wa Chisamariya pa chitsime. Nchifukwa, ngakhale kulankhula pabwalo kwanthawi yaitali ndi mkazi wina aliyense kungawonedwe moipa!a Koma Yesu sanalole maganizo a kumaloko kumuletsa iye kupereka umboni. Ntchito ya Mulungu inali yopatsa mpumulo. Iye anati: “Chakudya changa ndicho kuti ndichite chifuniro cha iye amene anandituma ine, ndi kutsiriza ntchito yake.” Chimwemwe chakuwona chivomerezo cha anthuwo, monga mkazi wa Chisamariya ndi ambiri a anthu a m’mudzimo, chinamukwaniritsa Yesu monga chakudya.—Yohane 4:4-42; 8:48.
-
-
Onjezerani Mtendere Wanu mwa Chidziwitso CholongosokaNsanja ya Olonda—1987
-
-
a Malinga ndi kunena kwa Talmud, arabi akale analangiza kuti: “Wophunzira sayenera kulankhula ndi mkazi mkhwalala.” Ngati mwambo umenewu unalipo mtsiku la Yesu, mwinamwake chingakhale chifukwa chimene ophunzira ake “anazizwa kuti anali kulankhula ndi mkazi.”—Yohane 4:27.
-