-
“Ndikachita Apilo kwa Kaisara!”Nsanja ya Olonda—2001 | December 15
-
-
Paulo anadziteteza mwa kutchula mfundo imodzi ndi imodzi. Anati: ‘Sindinayambitse chisokonezo ine. N’zoonadi kuti ndili m’gulu lomwe akuti ndi “mpatuko,” koma kukhala m’gulu limeneli kumatanthauza kusunga malamulo achiyuda. Ayuda ena a ku Asiya ndiwo anayambitsa chisokonezo. Ngati iwowo ali ndi dandaulo abwere adzanene.’ Paulo anasonyeza kuti mlanduwo unali wachipembedzo pakati pa Ayuda. Aroma anali kudziŵa zochepa chabe pa milandu yamtunduwu. Pozindikira mkwiyo umene Ayuda aliumawo anali nawo, Felike anaimitsa mlanduwo ndipo sanapereke Paulo kwa Ayuda omwe ankadzinenera kuti anali kudziŵa bwino kuweruza milandu yamtunduwo. Komanso sanamuweruze potsatira lamulo la Aroma kapenanso kum’masula. Palibe amene akanaumiriza Felike kuti aweruze mlanduwo. Kuwonjezera pofuna kukondera Ayudawo, Felike anaimitsa mlanduwo n’cholinga chinanso. Iye ankayembekezera kuti mwina Paulo am’patsa chiphuphu.—Machitidwe 24:10-19, 26.b
-
-
“Ndikachita Apilo kwa Kaisara!”Nsanja ya Olonda—2001 | December 15
-
-
b Kuchita zimenezi kunali koletsedwa. Buku lina limanena kuti: “Malinga ndi malamulo pankhani ya katangale, Lex Repetundarum, munthu aliyense waudindo ankaletsedwa kulandira ziphuphu n’cholinga chilichonse kaya kuti am’mange munthu kapena kum’masula, kuweruza kapena kusaweruza, kapena kutulutsa mkaidi m’ndende.”
-