Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Lidiya—Wopembedza Mulungu Ndiponso Wochereza Alendo
    Nsanja ya Olonda—1996 | September 15
    • Kulalikira kwa Paulo ku Filipi

      Pafupifupi chaka cha 50 C.E., Paulo kwanthaŵi yoyamba anafika ku Ulaya nayamba kulalikira ku Filipi.a Pamene anafika mumzinda watsopanowo, chinali chizoloŵezi cha Paulo kupita ku sunagoge kukalalikira choyamba kwa Ayuda ndi otembenuka amene anali kusonkhana komweko. (Yerekezerani ndi Machitidwe 13:4, 5, 13, 14; 14:1.) Komabe, malinga ndi kunena kwa ena, lamulo la Roma linaletsa Ayuda kutsata chipembedzo chawo mu “malo opatulika” a Filipi. Chifukwa chake, atagona momwemo “masiku ena,” patsiku la Sabata amishonalewo anapeza malo m’mbali mwa mtsinje kunja kwa mzindawo kumene ‘anaganizira kuti amapempherako.’ (Machitidwe 16:12, 13) Mwachionekere umenewu unali Mtsinje wa Gangites. Kumeneko amishonalewo anangopezako akazi, mmodzi wa iwo anali Lidiya.

  • Lidiya—Wopembedza Mulungu Ndiponso Wochereza Alendo
    Nsanja ya Olonda—1996 | September 15
    • a Pakati pa mizinda yofunika koposa ya Makedoniya, Filipi anali mudzi wotukuka wa asilikali wolamuliridwa ndi jus italicum (Lamulo Lachitaliyana). Lamulo limeneli linapatsa Afilipi zoyenera zolingana ndi zija zimene nzika za Roma zinali nazo.​—Machitidwe 16:9, 12, 21.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena