Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Analalikira Uthenga Wabwino ku Tesalonika Movutikira Kwambiri
    Nsanja ya Olonda—2012 | June 1
    • Iwo “anakhamukira kunyumba ya Yasoni [yemwe ankasunga Paulo m’nyumba mwake], kukafuna atumwiwo kuti awatulutsire ku gulu lachipolowelo.” Koma atalephera kum’peza Paulo, anapita kwa akuluakulu a mzindawo. Choncho “anakokera Yasoni ndi abale ena kwa olamulira a mzindawo, akufuula kuti: ‘Anthu awa amene abweretsa mavuto padziko lapansi kumene kuli anthu, tsopano akupezekanso kuno.’”​—Machitidwe 17:5, 6.

      Popeza mzinda wa Tesalonika unali likulu la chigawo cha Makedoniya, unkadzilamulira wokha pa zinthu zina ndi zina. Ena mwa anthu amene ankalamulira mzindawu anali anthu amene ankasankhidwa kusamalira nkhani zina ndi zina zochitika mumzindawu. ‘Olamulira a mzinda’b amenewa anali akuluakulu a boma ndipo anali ndi udindo waukulu wokhazikitsa bata mumzindamo komanso kuonetsetsa kuti simukuchitika zinthu zimene zingachititse kuti boma la Roma lilowererepo n’kuwalanda mwayi wochita zinthu zina. Choncho iwo ayenera kuti anakhumudwa atamva kuti pali anthu ena amene akuchita zinthu zimene zingasokoneze mtendere wa mumzindawu.

  • Analalikira Uthenga Wabwino ku Tesalonika Movutikira Kwambiri
    Nsanja ya Olonda—2012 | June 1
    • b M’mabuku achigiriki munalibe mawu amenewa. Komabe anthu anafukula zolemba zakale zokhala ndi mawu amenewa pamalo amene panali mzinda wa Tesalonika ndipo zina mwa zolembazi zinalembedwa m’nthawi ya atumwi. Zinthu zimenezi zimatsimikizira kuti nkhani za m’buku la Machitidwe ndi zolondola.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena